< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
הַלְלוּ ־ יָהּ ׀ אוֹדֶה יְהֹוָה בְּכׇל־לֵבָב בְּסוֹד יְשָׁרִים וְעֵדָֽה׃
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
גְּדֹלִים מַעֲשֵׂי יְהֹוָה דְּרוּשִׁים לְכׇל־חֶפְצֵיהֶֽם׃
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
הוֹד־וְהָדָר פׇּעֳלוֹ וְצִדְקָתוֹ עֹמֶדֶת לָעַֽד׃
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
זֵכֶר עָשָׂה לְנִפְלְאוֹתָיו חַנּוּן וְרַחוּם יְהֹוָֽה׃
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
טֶרֶף נָתַן לִירֵאָיו יִזְכֹּר לְעוֹלָם בְּרִיתֽוֹ׃
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
כֹּחַ מַעֲשָׂיו הִגִּיד לְעַמּוֹ לָתֵת לָהֶם נַחֲלַת גּוֹיִֽם׃
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
מַעֲשֵׂי יָדָיו אֱמֶת וּמִשְׁפָּט נֶאֱמָנִים כׇּל־פִּקּוּדָֽיו׃
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
סְמוּכִים לָעַד לְעוֹלָם עֲשׂוּיִם בֶּאֱמֶת וְיָשָֽׁר׃
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
פְּדוּת ׀ שָׁלַח לְעַמּוֹ צִוָּֽה־לְעוֹלָם בְּרִיתוֹ קָדוֹשׁ וְנוֹרָא שְׁמֽוֹ׃
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
רֵאשִׁית חׇכְמָה ׀ יִרְאַת יְהֹוָה שֵׂכֶל טוֹב לְכׇל־עֹֽשֵׂיהֶם תְּהִלָּתוֹ עֹמֶדֶת לָעַֽד׃

< Masalimo 111 >