< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Louez l'Éternel! Je célébrerai l'Éternel de tout mon cœur, dans le conseil des justes, et dans l'assemblée.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Les œuvres de l'Éternel sont grandes, recherchées de tous ceux qui y prennent plaisir.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Son œuvre n'est que splendeur et magnificence, et sa justice demeure à perpétuité.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Il a laissé la mémoire de ses prodiges. L'Éternel est miséricordieux et compatissant.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Il donne à vivre à ceux qui le craignent; il se souvient toujours de son alliance.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Il a fait connaître à son peuple la force de ses œuvres, en lui donnant l'héritage des nations.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Les œuvres de ses mains ne sont que justice et vérité, et tous ses commandements sont véritables.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Ils sont stables à jamais, à perpétuité, étant faits avec vérité et droiture.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Il a envoyé la rédemption à son peuple. Il a établi son alliance pour toujours. Son nom est saint et redoutable.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Le commencement de la sagesse, c'est la crainte de l'Éternel. Tous ceux qui pratiquent ses commandements sont vraiment sages. Sa louange demeure à toujours.

< Masalimo 111 >