< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Praise Yahweh. I will give thanks to Yahweh with my whole heart in the assembly of the upright, in their gathering.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
The works of Yahweh are great, eagerly awaited by all those who desire them.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
His work is majestic and glorious, and his righteousness endures forever.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
He does wonderful things that will be remembered; Yahweh is gracious and merciful.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
He gives food to his faithful followers. He will always call to mind his covenant.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
He showed his powerful works to his people in giving them the inheritance of the nations.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
The works of his hands are trustworthy and just; all his instructions are reliable.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
They are established forever, to be observed faithfully and properly.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
He gave victory to his people; he ordained his covenant forever; holy and awesome is his name.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
To honor Yahweh is the beginning of wisdom; those who carry out his instructions have good understanding. His praise endures forever.

< Masalimo 111 >