< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Praise ye Yah! I will give thanks unto Yahweh, with a whole heart, in the circle of the upright and the assembly.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Great are the works of Yahweh, sought out, by all who find pleasure therein.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Honourable and majestic, is his doing, and, his righteousness, standeth for aye.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
A memorial, hath he made by his wonders, Gracious and compassionate, is Yahweh.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Food, hath he given to them who revere him, He will remember, age-abidingly, his covenant.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
The might of his works, hath he declared to his people, that he may give them the inheritance of the nations.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
The works of his hands, are faithful and just, Firm are all his precepts;
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Upheld to futurity, to times age-abiding, done in faithfulness and equity.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Ransom, hath he sent to his people, He hath commanded, to times age-abiding, his covenant, Holy and reverend, is his Name.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
The beginning of wisdom, is the reverence of Yahweh, Good discretion, have all that do them, His praise, endureth for aye.

< Masalimo 111 >