< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Alleluia. I will confess to you, O Lord, with my whole heart, in the council of the just and in the congregation.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Great are the works of the Lord, exquisite in all his intentions.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Confession and magnificence are his work. And his justice remains from age to age.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
He has created a memorial to his wonders; he is a merciful and compassionate Lord.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
He has given food to those who fear him. He will be mindful of his covenant in every age.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
He will announce the virtue of his works to his people,
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
so that he may give them the inheritance of the nations. The works of his hands are truth and judgment.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
All his commands are faithful: confirmed from age to age, created in truth and fairness.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
He has sent redemption upon his people. He has commanded his covenant for all eternity. Holy and terrible is his name.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
The fear of the Lord is the beginning of wisdom. A good understanding is for all who do it. His praise remains from age to age.

< Masalimo 111 >