< Masalimo 111 >
1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Halleluja! jeg takker HERREN af hele mit Hjerte i Oprigtiges Kreds og Menighed!
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Store er HERRENS Gerninger, gennemtænkte til Bunds.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Hans Værk er Højhed og Herlighed, hans Retfærd bliver til evig Tid.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Han har sørget for, at hans Undere mindes, naadig og barmhjertig er HERREN.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Dem, der frygter ham, giver han Føde, han kommer for evigt sin Pagt i Hu.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Han viste sit Folk sine vældige Gerninger, da han gav dem Folkenes Eje.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Hans Hænders Værk er Sandhed og Ret, man kan lide paa alle hans Bud;
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
de staar i al Evighed fast, udført i Sandhed og Retsind.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Han sendte sit Folk Udløsning, stifted sin Pagt for evigt. Helligt og frygteligt er hans Navn.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
HERRENS Frygt er Visdoms Begyndelse; forstandig er hver, som øver den. Evigt varer hans Pris!