< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Jeg vil prise Herren af ganske Hjerte i de oprigtiges Raad og i Menigheden.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Herrens Gerninger ere store, de blive søgte af alle dem, som have Lyst til dem.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Hans Værk er Majestæt og Herlighed, og hans Retfærdighed bestaar alle Tider.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Han beskikkede en Ihukommelse om sine underfulde Gerninger; naadig og barmhjertig er Herren.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Han har givet dem Spise, som frygte ham, han kommer evindelig sin Pagt i Hu.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Han har ladet sine Gerningers Kraft forkynde for sit Folk, idet han har givet dem Hedningernes Arv.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Hans Hænders Gerninger ere Sandhed og Ret, alle hans Befalinger ere trofaste.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
De ere grundfaste altid og evindelig, de ere satte i Sandhed og Oprigtighed.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Han sendte sit Folk Forløsning, han stiftede sin Pagt for evigt; hans Navn er helligt og forfærdeligt.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Herrens Frygt er Visdoms Begyndelse, en god Klogskab hos alle dem, som gøre derefter; hans Pris bestaar altid.

< Masalimo 111 >