< Masalimo 111 >
1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
你們要讚美耶和華! 我要在正直人的大會中,並公會中, 一心稱謝耶和華。
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
耶和華的作為本為大; 凡喜愛的都必考察。
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
他所行的是尊榮和威嚴; 他的公義存到永遠。
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
他行了奇事,使人記念; 耶和華有恩惠,有憐憫。
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
他賜糧食給敬畏他的人; 他必永遠記念他的約。
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
他向百姓顯出大能的作為, 把外邦的地賜給他們為業。
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
他手所行的是誠實公平; 他的訓詞都是確實的,
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
是永永遠遠堅定的, 是按誠實正直設立的。
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
他向百姓施行救贖, 命定他的約,直到永遠; 他的名聖而可畏。
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
敬畏耶和華是智慧的開端; 凡遵行他命令的是聰明人。 耶和華是永遠當讚美的!