< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
你们要赞美耶和华! 我要在正直人的大会中,并公会中, 一心称谢耶和华。
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
耶和华的作为本为大; 凡喜爱的都必考察。
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
他所行的是尊荣和威严; 他的公义存到永远。
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
他行了奇事,使人记念; 耶和华有恩惠,有怜悯。
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
他赐粮食给敬畏他的人; 他必永远记念他的约。
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
他向百姓显出大能的作为, 把外邦的地赐给他们为业。
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
他手所行的是诚实公平; 他的训词都是确实的,
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
是永永远远坚定的, 是按诚实正直设立的。
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
他向百姓施行救赎, 命定他的约,直到永远; 他的名圣而可畏。
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
敬畏耶和华是智慧的开端; 凡遵行他命令的是聪明人。 耶和华是永远当赞美的!

< Masalimo 111 >