< Masalimo 11 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
To the chief Musician, [A Psalm] of David. In the LORD I put my trust: how say ye to my soul, Flee [as] a bird to your mountain?
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
For lo, the wicked bend [their] bow, they make ready their arrow upon the string, that they may privily shoot at the upright in heart.
3 Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
If the foundations be destroyed, what can the righteous do?
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
The LORD [is] in his holy temple, the LORD'S throne [is] in heaven: his eyes behold, his eyelids try the children of men.
5 Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
The LORD trieth the righteous: but the wicked and him that loveth violence his soul hateth.
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
Upon the wicked he shall rain snares, fire and brimstone, and a horrible tempest: [this shall be] the portion of their cup.
7 Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
For the righteous LORD loveth righteousness; his countenance beholdeth the upright.

< Masalimo 11 >