< Masalimo 11 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
[For the Chief Musician. By David.] In the LORD, I take refuge. How can you say to my soul, "Flee as a bird to your mountain."
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
For, look, the wicked bend their bows. They set their arrows on the strings, that they may shoot in darkness at the upright in heart.
3 Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
If the foundations are destroyed, what can the righteous do?
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
The LORD is in his holy temple. The LORD is on his throne in heaven. His eyes look upon the poor. His eyes examine the descendants of Adam.
5 Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
The LORD examines the righteous, but the wicked and the one who loves violence his soul hates.
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
On the wicked he will rain blazing coals; fire, sulfur, and scorching wind shall be the portion of their cup.
7 Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
For the LORD is righteous. He loves righteousness. The upright shall see his face.

< Masalimo 11 >