< Masalimo 11 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Mwa Yehova ine ndimathawiramo. Nanga mungathe bwanji kunena kwa ine kuti, “Thawira ku phiri lako ngati mbalame.
For the chief music-maker. Of David. In the Lord put I my faith; how will you say to my soul, Go in flight like a bird to the mountain?
2 Pakuti taona oyipa akunga mauta awo; ayika bwino mivi yawo pa zingwe za uta, pobisala pawo kuti alase olungama mtima.
See, the bows of the evil-doers are bent, they make ready their arrows on the cord, so that they may send them secretly against the upright in heart.
3 Tsono ngati maziko awonongeka, olungama angachite chiyani?”
If the bases are broken down, what is the upright man to do?
4 Yehova ali mʼNyumba yake yoyera; Yehova ali pa mpando wake waufumu kumwamba. Iye amayangʼanitsitsa ana a anthu; maso ake amawayesa.
The Lord is in his holy Temple, the Lord's seat is in heaven; his eyes are watching and testing the children of men.
5 Yehova amayesa olungama, koma moyo wake umadana ndi oyipa, amene amakonda zachiwawa.
The Lord puts the upright and the sinner to the test, but he has hate in his soul for the lover of violent acts.
6 Iye adzakhuthulira pa oyipa makala amoto ndi sulufule woyaka; mphepo yotentha idzakhala yowayenera.
On the evil-doer he will send down fire and flames, and a burning wind; with these will their cup be full.
7 Pakuti Yehova ndi wolungama, Iye amakonda chilungamo; ndipo anthu olungama adzaona nkhope yake.
For the Lord is upright; he is a lover of righteousness: the upright will see his face.