< Masalimo 109 >
1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
In finem, Psalmus David.
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
Deus laudem meam ne tacueris: quia os peccatoris, et os dolosi super me apertum est.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
Locuti sunt adversum me lingua dolosa, et sermonibus odii circumdederunt me: et expugnaverunt me gratis.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
Pro eo ut me diligerent, detrahebant mihi: ego autem orabam.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
Et posuerunt adversum me mala pro bonis: et odium pro dilectione mea.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Constitue super eum peccatorem: et diabolus stet a dextris eius.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Cum iudicatur, exeat condemnatus: et oratio eius fiat in peccatum.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Fiant dies eius pauci: et episcopatum eius accipiat alter.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Fiant filii eius orphani: et uxor eius vidua.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
Nutantes transferantur filii eius, et mendicent: et eiiciantur de habitationibus suis.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
Scrutetur fœnerator omnem substantiam eius: et diripiant alieni labores eius.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Non sit illi adiutor: nec sit qui misereatur pupillis eius.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Fiant nati eius in interitum: in generatione una deleatur nomen eius.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
In memoriam redeat iniquitas patrum eius in conspectu Domini: et peccatum matris eius non deleatur.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Fiant contra Dominum semper, et dispereat de terra memoria eorum:
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
pro eo quod non est recordatus facere misericordiam.
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Et persecutus est hominem inopem, et mendicum, et compunctum corde mortificare.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
Et dilexit maledictionem, et veniet ei: et noluit benedictionem, et elongabitur ab eo. Et induit maledictionem sicut vestimentum, et intravit sicut aqua in interiora eius, et sicut oleum in ossibus eius.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Fiat ei sicut vestimentum, quo operitur: et sicut zona, qua semper præcingitur.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
Hoc opus eorum, qui detrahunt mihi apud Dominum: et qui loquuntur mala adversus animam meam.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
Et tu Domine, Domine, fac mecum propter nomen tuum: quia suavis est misericordia tua.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
Libera me quia egenus, et pauper ego sum: et cor meum conturbatum est intra me.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
Sicut umbra cum declinat, ablatus sum: et excussus sum sicut locustæ.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Genua mea infirmata sunt a ieiunio: et caro mea immutata est propter oleum.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
Et ego factus sum opprobrium illis: viderunt me, et moverunt capita sua.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Adiuva me Domine Deus meus: salvum me fac secundum misericordiam tuam.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
Et sciant quia manus tua hæc: et tu Domine fecisti eam.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Maledicent illi, et tu benedices: qui insurgunt in me, confundantur: servus autem tuus lætabitur.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Induantur qui detrahunt mihi, pudore: et operiantur sicut diploide confusione sua.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
Confitebor Domino nimis in ore meo: et in medio multorum laudabo eum.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Quia astitit a dextris pauperis, ut salvam faceret a persequentibus animam meam.