< Masalimo 109 >
1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
Salmo di Davide, [dato] al Capo de' Musici O DIO della mia lode, non tacere;
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
Perciocchè la bocca dell'empio e la bocca di frode si sono aperte contro a me; Hanno parlato meco con lingua bugiarda;
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
E mi hanno assediato con parole d'odio; E mi hanno fatta guerra senza cagione.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
In vece dell'amore che ho loro portato, mi sono stati avversari; Ed io [ho loro renduta] preghiera.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
Essi mi hanno renduto male per bene, E odio per lo mio amore.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Costituisci il maligno sopra lui; E fa' che Satana gli stia alla destra.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Quando sarà giudicato, esca condannato; E la sua preghiera [gli] torni in peccato.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Sieno i suoi giorni pochi; Un altro prenda il suo ufficio.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Sieno i suoi figliuoli orfani, E la sua moglie vedova.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
E vadano i suoi figliuoli del continuo vagando; E mendichino, ed accattino, [uscendo fuor] de' lor casolari.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
L'usuraio tenda la rete a tutto ciò ch'egli ha; E rubino gli strani le sue fatiche.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Non siavi alcuno che stenda la [sua] benignità inverso lui; E non vi sia chi abbia pietà de' suoi orfani.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Sieno distrutti i suoi discendenti; Sia cancellato il lor nome nella seconda generazione.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
Sia ricordata l'iniquità de' suoi padri appo il Signore; E il peccato di sua madre non sia cancellato.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Sieno [que' peccati] del continuo nel cospetto del Signore; E stermini egli d'in su la terra la memoria di essi.
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
Perciocchè egli non si è ricordato d'usar benignità, Ed ha perseguitato l'uomo povero, ed afflitto, E tribolato di cuore, per uccider[lo].
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Poichè egli ha amata la maledizione, vengagli; E [poichè] non si è compiaciuto nella benedizione, allontanisi ella da lui.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
E sia vestito di maledizione, come del suo manto; Ed entri quella come acqua nelle sue interiora, E come olio nelle sue ossa.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Siagli quella a guisa di vestimento, [del quale] egli sia avvolto; Ed a guisa di cintura, della quale sempre sia cinto.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
[Tal] sia, da parte del Signore, la ricompensa de' miei avversari, E di quelli che parlano male contro all'anima mia.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
Ma tu, o Signore Iddio, opera inverso me, per amor del tuo Nome; Liberami, perciocchè la tua benignità [è] buona.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
Perciocchè io sono afflitto, e povero; E il mio cuore è piagato dentro di me.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
Io me ne vo, come l'ombra quando dichina; Io sono agitato come una locusta.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Le mie ginocchia vacillano per li [miei] digiuni; E la mia carne è dimagrata, e non ha [più] grassezza alcuna.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
Ed anche son loro in vituperio; [Quando] mi veggono, scuotono la testa.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Aiutami, Signore Iddio mio; Salvami secondo la tua benignità.
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
E sappiano che questo [è] la tua mano, [E che] tu, Signore, hai fatto questo.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Essi malediranno, e tu benedirai; Si sono innalzati, ma saran confusi, Ed il tuo servitore si rallegrerà.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Sieno i miei avversari vestiti di vituperio, Ed avvolti della lor vergogna, come di un mantello.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
Io celebrerò altamente il Signore colla mia bocca; E lo loderò in mezzo de' grandi.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Perciocchè egli sta alla destra del povero, Per salvar[lo] da quelli che lo condannano a morte.