< Masalimo 109 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
For the Chief Musician. A Psalm by David. God of my praise, don’t remain silent,
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
for they have opened the mouth of the wicked and the mouth of deceit against me. They have spoken to me with a lying tongue.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
They have also surrounded me with words of hatred, and fought against me without a cause.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
In return for my love, they are my adversaries; but I am in prayer.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
They have rewarded me evil for good, and hatred for my love.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Set a wicked man over him. Let an adversary stand at his right hand.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
When he is judged, let him come out guilty. Let his prayer be turned into sin.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Let his days be few. Let another take his office.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Let his children be fatherless, and his wife a widow.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
Let his children be wandering beggars. Let them be sought from their ruins.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
Let the creditor seize all that he has. Let strangers plunder the fruit of his labour.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Let there be no one to extend kindness to him, neither let there be anyone to have pity on his fatherless children.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Let his posterity be cut off. In the generation following let their name be blotted out.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
Let the iniquity of his fathers be remembered by the LORD. Don’t let the sin of his mother be blotted out.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Let them be before the LORD continually, that he may cut off their memory from the earth;
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
because he didn’t remember to show kindness, but persecuted the poor and needy man, the broken in heart, to kill them.
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Yes, he loved cursing, and it came to him. He didn’t delight in blessing, and it was far from him.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
He clothed himself also with cursing as with his garment. It came into his inward parts like water, like oil into his bones.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Let it be to him as the clothing with which he covers himself, for the belt that is always around him.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
This is the reward of my adversaries from the LORD, of those who speak evil against my soul.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
But deal with me, GOD the Lord, for your name’s sake, because your loving kindness is good, deliver me;
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
for I am poor and needy. My heart is wounded within me.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
I fade away like an evening shadow. I am shaken off like a locust.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
My knees are weak through fasting. My body is thin and lacks fat.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
I have also become a reproach to them. When they see me, they shake their head.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Help me, LORD, my God. Save me according to your loving kindness;
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
that they may know that this is your hand; that you, LORD, have done it.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
They may curse, but you bless. When they arise, they will be shamed, but your servant shall rejoice.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Let my adversaries be clothed with dishonour. Let them cover themselves with their own shame as with a robe.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
I will give great thanks to the LORD with my mouth. Yes, I will praise him amongst the multitude.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
For he will stand at the right hand of the needy, to save him from those who judge his soul.

< Masalimo 109 >