< Masalimo 109 >
1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
For the Chief Musician. A Psalm of David. Hold not thy peace, O God of my praise;
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
For the mouth of the wicked and the mouth of deceit have they opened against me: they have spoken unto me with a lying tongue.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
They compassed me about also with words of hatred, and fought against me without a cause.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
For my love they are my adversaries: but I [give myself unto] prayer.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
And they have rewarded me evil for good, and hatred for my love.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Set thou a wicked man over him: and let an adversary stand at his right hand.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
When he is judged, let him come forth guilty; and let his prayer be turned into sin.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Let his days be few; [and] let another take his office.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Let his children be fatherless, and his wife a widow.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
Let his children be vagabonds, and beg; and let them seek [their bread] out of their desolate places.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
Let the extortioner catch all that he hath; and let strangers make spoil of his labour.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Let there be none to extend mercy unto him; neither let there be any to have pity on his fatherless children.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Let his posterity be cut off; in the generation following let their name be blotted out.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
Let the iniquity of his fathers be remembered with the LORD; and let not the sin of his mother be blotted out.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Let them be before the LORD continually, that he may cut off the memory of them from the earth.
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
Because that he remembered not to shew mercy, but persecuted the poor and needy man, and the broken in heart, to slay [them].
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Yea, he loved cursing, and it came unto him; and he delighted not in blessing, and it was far from him.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
He clothed himself also with cursing as with his garment, and it came into his inward parts like water, and like oil into his bones. Let it be unto him as the raiment
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
wherewith he covereth himself, and for the girdle wherewith he is girded continually.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
This is the reward of mine adversaries from the LORD, and of them that speak evil against my soul.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
But deal thou with me, O GOD the Lord, for thy name’s sake: because thy mercy is good, deliver thou me,
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
For I am poor and needy, and my heart is wounded within me.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
I am gone like the shadow when it declineth: I am tossed up and down as the locust.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
My knees are weak through fasting; and my flesh faileth of fatness.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
I am become also a reproach unto them: when they see me, they shake their head.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Help me, O LORD my God; O save me according to thy mercy:
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
That they may know that this is thy hand; [that] thou, LORD, hast done it.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Let them curse, but bless thou: when they arise, they shall be ashamed, but thy servant shall rejoice.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Let mine adversaries be clothed with dishonour, and let them cover themselves with their own shame as with a mantle.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
I will give great thanks unto the LORD with my mouth; yea, I will praise him among the multitude.
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
For he shall stand at the right hand of the needy, to save him from them that judge his soul.