< Masalimo 109 >

1 Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
Přednímu zpěváku, žalm Davidův. Ó Bože chvály mé, nečiň se neslyše.
2 pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
Nebo ústa nešlechetného a ústa lstivá proti mně se otevřela, mluvili proti mně jazykem lživým.
3 Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
A slovy jizlivými osočili mne, válčí proti mně beze vší příčiny.
4 Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
Protivili mi se za mé milování, ješto jsem se za ně modlíval.
5 Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
Odplacují se mi zlým za dobré, a nenávistí za milování mé.
6 Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
Postav nad ním bezbožníka, a protivník ať mu stojí po pravici.
7 Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
Když před soudem stane, ať zůstane za nešlechetného, a prosba jeho budiž jemu k hříchu.
8 Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
Budiž dnů jeho málo, a úřad jeho vezmi jiný.
9 Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
Buďtež děti jeho sirotci, a žena jeho vdovou.
10 Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
Buďtež běhouni a tuláci synové jeho, žebřete, vyhnáni jsouce z poustek svých.
11 Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
Přitáhni k sobě lichevník všecko, cožkoli má, a úsilé jeho rozchvátejte cizí.
12 Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
Nebudiž, kdo by mu chtěl milosrdenství prokázati, aniž buď, kdo by se smiloval nad sirotky jeho.
13 Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
Potomci jeho z kořen vyťati buďte, v druhém kolenu vyhlazeno buď jméno jejich.
14 Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
Přijdiž na pamět nepravost předků jeho před Hospodinem, a hřích matky jeho nebuď shlazen.
15 Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
Buďtež před Hospodinem ustavičně, až by vyhladil z země památku jejich,
16 Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
Proto že nepamatoval, aby činil milosrdenství, ale protivenství činil člověku chudému a nuznému a sevřenému bolestí srdce, aby jej zamordoval.
17 Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
Poněvadž miloval zlořečení, nechať přijde na něj; neměl líbosti v požehnání, nechať se vzdálí od něho.
18 Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
A tak budiž oblečen v zlořečenství jako v svůj oděv, a ať vejde do vnitřností jeho jako voda, a jako olej do kostí jeho.
19 Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
Budiž jemu to jako plášť k přiodívání, a jako pás k ustavičnému opasování.
20 Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
Taková mzda přijdiž mým protivníkům od Hospodina, a mluvícím zlé věci proti duši mé.
21 Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
Ty pak, Hospodine Pane, nalož se mnou laskavě pro jméno své, nebo dobré jest milosrdenství tvé; vytrhni mne.
22 Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
Jsemť zajisté chudý a nuzný, a srdce mé raněno jest u vnitřnostech mých.
23 Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
Jako stín, když se nachyluje, ucházeti musím; honí se za mnou jako za kobylkou.
24 Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
Kolena má klesají postem, a tělo mé vyschlo z tučnosti.
25 Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
Nadto jsem jim za posměch; když mne uhlédají, potřásají hlavami svými.
26 Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
Spomoz mi, ó Hospodine Bože můj, zachovej mne podlé milosrdenství svého,
27 Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
Tak aby poznati mohli, že jest to ruka tvá, a že jsi ty, Hospodine, učinil to.
28 Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
Nechť oni jakkoli zlořečí, ty dobrořeč; kteříž povstali, nechť se zastydí, aby se veselil služebník tvůj.
29 Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
Buďtež oblečeni protivníci moji v zahanbení, a nechť se odějí jako pláštěm hanbou svou.
30 Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
Slaviti budu Hospodina velice ústy svými, a u prostřed mnohých chváliti jej budu,
31 Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.
Proto že stojí po pravici nuznému, aby ho zachoval od těch, kteříž odsuzují život jeho.

< Masalimo 109 >