< Masalimo 108 >
1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Готово је срце моје, Боже; певаћу и хвалићу заједно са славом својом.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Прени се псалтире и гусле, устаћу рано.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Славићу Тебе, Господе, по народима, појаћу Теби по племенима.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Јер је сврх небеса милост Твоја и до облака истина Твоја.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Узвиси се више небеса, Боже, и по свој земљи нека буде слава Твоја!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Да би се избавили мили Твоји, помози десницом својом, и услиши ме.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Бог рече у светињи својој: "Веселићу се, разделићу Сихем, и долину Сокот размерићу.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Мој је Галад, мој је Манасија, Јефрем је крепост главе моје, Јуда скиптар мој.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Моав је чаша из које се умивам, Едому ћу пружити обућу своју; над земљом филистејском попеваћу."
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Ко ће ме одвести у тврди град? Ко ће ме отпратити до Едома?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Зар нећеш Ти, Боже, који си нас одбацио, и не идеш, Боже, с војскама нашим?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Дај нам помоћ у тескоби, одбрана је човечија узалуд.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Богом смо јаки; Он гази непријатеље наше.