< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Гата ымь есте инима сэ кынте, Думнезеуле! Вой кынта, вой суна дин инструментеле меле; ачаста есте слава мя!
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Дештептаци-вэ, алэутэ ши харпэ! Мэ вой трези ын зорь де зи.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Те вой лэуда принтре попоаре, Доамне, Те вой кынта принтре нямурь.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Кэч маре есте бунэтатя Та ши се ыналцэ май пресус де черурь, яр крединчошия Та пынэ ла норь.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Ыналцэ-Те песте черурь, Думнезеуле, ши фие слава Та песте тот пэмынтул!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Пентру ка пряюбиций Тэй сэ фие избэвиць, скапэ-не прин дряпта Та ши аскултэ-не!
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Думнезеу а ворбит ын сфинцения Луй: „Вой бируи, вой ымпэрци Сихемул, вой мэсура валя Сукот;
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
ал Меу есте Галаадул, ал Меу Манасе; Ефраим есте ынтэритура капулуй Меу ши Иуда, тоягул Меу де кырмуире;
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Моаб есте лигянул ын каре Мэ спэл; Ымь арунк ынкэлцэминтя асупра Едомулуй; стриг де букурие асупра цэрий филистенилор!”
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Чине мэ ва дуче ын четатя ынтэритэ? Чине мэ ва дуче ла Едом?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Оаре ну Ту, Думнезеуле, каре не-ай лепэдат ши каре ну врей сэ май ешь, Думнезеуле, ку оштириле ноастре?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Дэ-не ажутор ын неказ, кэч задарник есте ажуторул омулуй.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Ку Думнезеу вом фаче марь испрэвь; Ел ва здроби пе врэжмаший ноштри.

< Masalimo 108 >