< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Preparado está o meu coração, ó Deus; cantarei e direi salmos até com a minha glória.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Desperta-te, saltério e harpa; eu mesmo despertarei ao romper da alva.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Louvar-te-ei entre os povos, Senhor, e a ti cantarei salmos entre as nações.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Porque a tua benignidade se estende até aos céus, e a tua verdade chega até às mais altas nuvens.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Exalta-te sobre os céus, ó Deus, e a tua glória sobre toda a terra,
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Para que sejam livres os teus amados: salva-nos com a tua dextra, e ouve-nos.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Deus falou na sua santidade: eu me regozijarei; repartirei a Sichem, e medirei o vale de Succoth.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Meu é Galaad, meu é Manassés; e Ephraim a força da minha cabeça, Judá o meu legislador,
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab o meu vaso de lavar: sobre Edom lançarei o meu sapato, sobre a Palestina jubilarei.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Quem me levará à cidade forte? Quem me guiará até Edom?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Porventura não serás tu, ó Deus, que nos rejeitaste? E não sairás, ó Deus, com os nossos exércitos?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Dá-nos auxílio para sair da angústia, porque vão é o socorro da parte do homem.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Em Deus faremos proezas, pois ele calcará aos pés os nossos inimigos.

< Masalimo 108 >