< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Pieśń psalmu samego Dawida. Gotowe jest serce moje, Boże! śpiewać i wysławiać cię będę, także i chwała moja.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Ocućże się lutnio i harfo! gdy na świtaniu powstaję.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Wysławiać cię będę między ludźmi, Panie! a będęć śpiewał między narodami.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Albowiem większe jest nad niebiosa miłosierdzie twoje, i aż pod obłoki prawda twoja.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Wywyszże się nad niebiosa, o Boże! a nad wszystkę ziemię chwała twoja.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Niech będą wybawieni umiłowami twoi; zachowajże ich prawicą swoją, a wysłuchaj mię.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Bóg mówił przez świętobliwość swoję; dlatego się weselić będę, że rozdzielę Sychem, a dolinę Sukkot rozmierzę.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Mojeć jest Galaad, mój i Manases, a Efraim mocą głowy mojej, Juda zakonodawca mój.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab jest miednicą do umywania mego, na Edoma porzucę obuwie moje: przeciwko Filistynom trąbić będę.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Któż mię zaprowadzi do miasta obronnego? Któż mię przywiedzie aż do ziemi edomskiej?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Izali nie ty, o Boże! któryś nas był odrzucił, a nie wychodziłeś, o Boże! z wojskami naszemi?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Dajże nam pomoc z ucisku; albowiem omylna jest pomoc ludzka.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
W Bogu sobie mężnie poczynać będziemy, a on podepcze nieprzyjaciół naszych.

< Masalimo 108 >