< Masalimo 108 >
1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Nyanyian. Mazmur Daud. Aku percaya teguh, ya Allah, aku mau menyanyi dan memuji Engkau. Hai bangunlah, jiwaku!
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Hai bangunlah, gambus dan kecapi! Aku mau membangunkan fajar.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
TUHAN, aku mau bersyukur kepada-Mu di antara bangsa-bangsa. Kuingin menyanyikan pujian bagi-Mu di antara umat manusia.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Sebab kasih-Mu besar sampai ke langit dan kesetiaan-Mu sampai ke awan-awan.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Ya Allah, tunjukkanlah keagungan-Mu di langit, dan kemuliaan-Mu di seluruh bumi.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Selamatkanlah kami dengan kuasa-Mu, jawablah doa kami, supaya orang-orang yang Kaukasihi diselamatkan.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Dari kediaman-Nya yang suci Allah berkata, "Aku mau bersorak dan membagi-bagikan tanah Sikhem, Lembah Sukot akan Kuundi.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Gilead dan Manasye adalah milik-Ku, Efraim topi baja-Ku, dan Yehuda tongkat kerajaan-Ku.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Tapi Moab adalah tempat pembasuhan kaki-Ku; Aku bersorak kemenangan atas Filistea. Kepada Edom Kulemparkan kasut-Ku, sebagai tanda bahwa ia milik-Ku."
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Siapa akan membawa aku ke Edom? Siapa menuntun aku ke kota berkubu itu?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Ya Allah, tidakkah Engkau ikut bersama kami? Tidakkah Engkau maju bersama tentara kami?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Tolonglah kami terhadap musuh, sebab bantuan manusia tidak berguna.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Bersama Allah, kita akan gagah perkasa; Dialah yang mengalahkan musuh kita.