< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Cantique. Psaume de David. Mon cœur reste ferme, ô Dieu! Je puis chanter, célébrer tes louanges; c’est là mon honneur.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Réveillez-vous, ô luth et harpe! Je veux réveiller l’aurore.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Je te louerai parmi les nations, ô Seigneur, je te chanterai parmi les peuples.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Car ta grâce s’élève par-dessus les cieux, et ta bonté atteint jusqu’au firmament.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Montre ta grandeur, ô Dieu, qui dépasse les cieux; que ta gloire brille sur toute la terre!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Afin que tes bien-aimés échappent au danger, secours-nous avec ta droite, et exauce-moi!
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
L’Eternel l’a annoncé en son sanctuaire: "Je triompherai, je veux m’adjuger Sichem, mesurer au cordeau la vallée de Souccot.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
A moi Galaad! à moi Manassé! Ephraïm est la puissante sauvegarde de ma tête, Juda est mon sceptre.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab est le bassin où je me lave; sur Edom, je jette ma sandale, je triomphe du pays des Philistins."
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Qui me conduira à la ville forte? Qui saura me mener jusqu’à Edom?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Ne sera-ce pas toi, ô Dieu, toi qui nous avais délaissés, qui ne faisais plus campagne avec nos armées?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Prête-nous secours contre l’adversaire, puisque trompeuse est l’aide de l’homme.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Avec Dieu, nous ferons des prouesses: c’est lui qui écrasera nos ennemis.

< Masalimo 108 >