< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Cantique. Psaume de David. Mon cœur est affermi, ô Dieu, je chanterai et ferai retentir de joyeux instruments. Debout, ma gloire!
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Éveillez-vous, ma lyre et ma harpe! Que j’éveille l’aurore!
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Je te louerai parmi les peuples, Yahweh, je te chanterai parmi les nations.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Car ta bonté s’élève au-dessus des cieux, et ta fidélité jusqu’aux nues.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Élève-toi au-dessus des cieux, ô Dieu; que ta gloire brille sur toute la terre!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Afin que tes bien-aimés soient délivrés, sauve par ta droite et exauce-moi.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Dieu a parlé dans sa sainteté: « Je tressaillirai de joie! J’aurai Sichem en partage, je mesurerai la vallée de Succoth.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Galaad est à moi, à moi Manassé; Ephraïm est l’armure de ma tête, et Judas mon sceptre.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab est le bassin où je me lave; sur Edom je jette ma sandale; sur la terre des Philistins je pousse des cris de joie. »
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Qui me mènera à la ville forte! Qui me conduira à Edom?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
N’est-ce pas toi, ô Dieu, qui nous avais rejetés, ô Dieu qui ne sortais plus avec nos armées?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Prête-nous ton secours contre l’oppresseur! Le secours de l’homme n’est que vanité.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Avec Dieu nous accomplirons des exploits; il écrasera nos ennemis.

< Masalimo 108 >