< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Une chanson. Un psaume de David. Mon cœur est inébranlable, Dieu. Je chanterai et je ferai de la musique avec mon âme.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Réveillez-vous, harpe et lyre! Je vais réveiller l'aube.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Je te louerai, Yahvé, parmi les nations. Je chanterai tes louanges parmi les peuples.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Car ta bonté est grande au-dessus des cieux. Votre fidélité s'étend jusqu'aux cieux.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Sois exalté, Dieu, au-dessus des cieux! Que ta gloire soit sur toute la terre.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Pour que ton bien-aimé soit délivré, sauve de ta main droite, et réponds-nous.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Dieu a parlé depuis son sanctuaire: « En triomphe, Je diviserai Sichem, et je mesurerai la vallée de Succoth.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Galaad est à moi. Manassé est à moi. Ephraïm aussi est mon casque. Juda est mon sceptre.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab est mon pot de lavage. Je jetterai ma sandale sur Edom. Je crierai sur la Philistie. »
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Qui me fera entrer dans la ville fortifiée? Qui me conduira à Edom?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Ne nous as-tu pas rejetés, Dieu? Tu ne sors pas, Dieu, avec nos armées.
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Donne-nous du secours contre l'ennemi, car l'aide de l'homme est vaine.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Par Dieu, nousferons preuve de courage, car c'est lui qui écrasera nos ennemis.

< Masalimo 108 >