< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Psalmi, Davidin veisu. Jumala! minun sydämeni on valmis: minä veisaan ja kiitän, niin myös minun kunniani.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Nouse, psaltari ja kantele; minä nousen varhain.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Sinua, Herra, minä kiitän kansain seassa: minä veisaan sinulle kiitosta sukukunnissa.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
Sillä sinun armos on suuri ylitse taivasten, ja sinun totuutes hamaan pilviin asti.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Korota sinuas, Jumala, taivasten ylitse ja kunnias kaiken maan ylitse,
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Että sinun rakkaat ystäväs vapaaksi tulisivat; auta oikialla kädelläs, ja kuule minun rukoukseni.
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Jumala on puhunut pyhässänsä, siitä minä iloitsen: minä jaan Sikemin, ja mittaan Sukkotin laakson.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Gilead on minun, Manasse on myös minun, ja Ephraim on minun pääni väkevyys: Juuda on minun päämieheni;
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab on minun pesinastiani, minä venytän kenkäni Edomin päälle: Philistealaisten ylitse minä iloitsen.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Kuka vie minua vahvaan kaupunkiin? kuka vie minua Edomiin?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Etkös sinä, Jumala, joka meitä heittänyt olet pois? Ja etkös mene ulos, Jumala, meidän sotaväkemme kanssa?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Saata meille apua tuskissamme; sillä ihmisten apu on turha.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Jumalassa me tahdomme urhoollisia töitä tehdä; ja hän polkee meidän vihollisemme alas.

< Masalimo 108 >