< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
“A psalm of David.” O God! my heart is strengthened! I will sing and give thanks.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Awake, my soul! awake, my psaltery and harp! I will wake with the early dawn.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
I will praise thee, O LORD! among the nations; I will sing to thee among the peoples!
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
For thy mercy reacheth to the heavens, And thy truth above the clouds.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Exalt thyself, O God! above the heavens, And thy glory above all the earth!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
That thy beloved ones may be delivered, Save with thy right hand, and answer me!
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
God promiseth in his holiness; I will rejoice; I shall yet divide Shechem, And measure out the valley of Succoth;
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Gilead shall be mine, and mine Manasseh; Ephraim shall be my helmet, And Judah my sceptre.
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab shall be my washbowl; Upon Edom shall I cast my shoe; I shall triumph over Philistia.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who will bring me to the strong city? Who will lead me into Edom?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Wilt not thou, O God! who didst forsake us, Who didst not go forth with our armies?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Give us thine aid in our distress, For vain is the help of man!
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Through God we shall do valiantly; For he will tread down our enemies.

< Masalimo 108 >