< Masalimo 108 >
1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Song of a Psalm by David. O God, my heart is ready, my heart is ready; I will sing and sing psalms with my glory.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Awake, psaltery and harp; I will awake early.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
I will give thanks to thee, O Lord, among the people; I will sing praise to thee among the Gentiles.
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
For thy mercy is great above the heavens, and thy truth [reaches] to the clouds.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Be thou exalted, O God, above the heavens; and thy glory above all the earth.
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
That thy beloved [ones] may be delivered, save with thy right hand, and hear me. God has spoken in his sanctuary;
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
I will be exalted, and will divide Sicima, and will measure out the valley of tents.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Galaad is mine; and Manasses is mine; and Ephraim is the help of mine head; Judas is my king;
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab is the caldron of my hope; over Idumea will I cast my sandal; the Philistines are made subject to me.
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Who will bring me into the fortified city? or who will guide me to Idumea?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Wilt not thou, O God, who hast rejected us? and wilt not thou, O God, go forth with our hosts?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Give us help from tribulation: for vain is the help of man.
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
Through God we shall do valiantly; and he will bring to nought our enemies.