< Masalimo 108 >

1 Nyimbo. Salimo la Davide. Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu; ndidzayimba nyimbo, inde ndidzayimba nyimbo zotamanda ndi moyo wanga wonse.
Pjesma. Psalam. Davidov. Moje je srce sigurno, Bože, sigurno je srce moje: pjevat ću i svirati.
2 Dzukani, zeze ndi pangwe! Ine ndidzadzutsa mʼbandakucha.
Probudi se, dušo moja! Probudi se, harfo i citaro! Probudit ću zoru jutarnju.
3 Ndidzakutamandani Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba za Inu pakati pa anthu a mitundu ina.
Hvalit ću te, Jahve, među narodima, među pucima tebi ću pjevati,
4 Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kutalika kwake kuposa kumwamba; kukhulupirika kwanu kumafika mlengalenga.
jer do neba je dobrota tvoja, do oblaka tvoja vjernost.
5 Kwezekani Inu Mulungu, kuposa mayiko akumwamba, ndipo ulemerero wanu uphimbe dziko lonse lapansi.
Uzvisi se, Bože, nad nebesa, slava tvoja nek' je nad svom zemljom!
6 Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
Da ti se ljubimci izbave, desnicom pomozi, usliši nas!
7 Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwachipambano Ine ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayesa chigwa cha Sukoti.
Bog reče u svom Svetištu: “Šekem ću razdijelit' kličući, dolinu ću Sukot izmjeriti.
8 Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu.
Moj je Gilead, moj Manaše, Efrajim mi kaciga, Judeja žezlo moje!
9 Mowabu ndi mbale yanga yosambiramo ndidzaponya nsapato zanga pa Edomu; ndidzafuwula mopambana pa Filisitiya.”
Moab je sud iz kojeg se umivam, na Edom ću baciti obuću, nad Filistejcem slaviti pobjedu!”
10 Ndani adzandifikitsa ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
Tko će me dovesti do utvrđena grada, tko će me dovesti do Edoma?
11 Kodi sindinu Mulungu, Inu amene mwatikana ndipo simuperekezanso magulu athu ankhondo?
Zar nećeš ti, o Bože, što nas odbaci? Zar nećeš više, Bože, sa četama našim?
12 Tithandizeni ife kulimbana ndi mdani, pakuti thandizo la munthu ndi lopanda pake.
Pomozi nam protiv dušmana, jer je ljudska pomoć ništavna!
13 Chifukwa cha Mulungu wathu, ife tidzapeza chipambano, ndipo adzapondereza pansi adani athu.
S Božjom pomoću hrabro ćemo se boriti, Bog će zgaziti naše dušmane.

< Masalimo 108 >