< Masalimo 107 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
RAB'be şükredin, çünkü O iyidir, Sevgisi sonsuzdur.
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
Böyle desin RAB'bin kurtardıkları, Düşman pençesinden özgür kıldıkları,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko, kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
Doğudan, batıdan, kuzeyden, güneyden, Bütün ülkelerden topladıkları.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu, osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
Issız çöllerde dolaştılar, Yerleşecekleri kente giden bir yol bulamadılar.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu, ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
Aç, susuz, Sefil oldular.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
O zaman sıkıntı içinde RAB'be yakardılar, RAB kurtardı onları dertlerinden.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
Yerleşecekleri bir kente varıncaya dek, Onlara doğru yolda öncülük etti.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
Şükretsinler RAB'be sevgisi için, İnsanlar yararına yaptığı harikalar için.
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
Çünkü O susamış canın susuzluğunu giderir, Aç canı iyiliklerle doyurur.
10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu, amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
Zincire vurulmuş, acıyla kıvranan tutsaklar, Karanlıkta, zifiri karanlıkta oturmuştu.
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
Çünkü Tanrı'nın buyruklarına karşı çıkmışlardı, Küçümsemişlerdi Yüceler Yücesi'nin öğüdünü.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga; anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
Ağır işlerle hayatı onlara zehir etti, Çöktüler, yardım eden olmadı.
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
O zaman sıkıntı içinde RAB'be yakardılar, RAB kurtardı onları dertlerinden;
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu ndipo anadula maunyolo awo.
Çıkardı karanlıktan, zifiri karanlıktan, Kopardı zincirlerini.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
Şükretsinler RAB'be sevgisi için, İnsanlar yararına yaptığı harikalar için!
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
Çünkü tunç kapıları kırdı, Demir kapı kollarını parçaladı O.
17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira, ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
Cezalarını buldu aptallar, Suçları, isyanları yüzünden.
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
İğrenir olmuşlardı bütün yemeklerden, Ölümün kapılarına yaklaşmışlardı.
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
O zaman sıkıntı içinde RAB'be yakardılar, RAB kurtardı onları dertlerinden.
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa; anawalanditsa ku manda.
Sözünü gönderip iyileştirdi onları, Kurtardı ölüm çukurundan.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Şükretsinler RAB'be sevgisi için, İnsanlar yararına yaptığı harikalar için!
22 Apereke nsembe yachiyamiko ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
Şükran kurbanları sunsunlar Ve sevinç çığlıklarıyla duyursunlar O'nun yaptıklarını!
23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi; Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
Gemilerle denize açılanlar, Okyanuslarda iş yapanlar,
24 Anaona ntchito za Yehova, machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
RAB'bin işlerini, Derinliklerde yaptığı harikaları gördüler.
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho imene inabweretsa mafunde ataliatali.
Çünkü O buyurunca şiddetli bir fırtına koptu, Dalgalar şaha kalktı.
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya; pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
Göklere yükselip diplere indi gemiler, Sıkıntıdan canları burunlarına geldi gemicilerin,
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera; anali pa mapeto a moyo wawo.
Sarhoş gibi sallanıp sendelediler, Ustalıkları işe yaramadı.
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
O zaman sıkıntı içinde RAB'be yakardılar, RAB kurtardı onları dertlerinden.
29 Yehova analetsa namondwe, mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
Fırtınayı limanlığa çevirdi, Yatıştı dalgalar;
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata, ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
Rahatlayınca sevindiler, Diledikleri limana götürdü RAB onları.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Şükretsinler RAB'be sevgisi için, İnsanlar yararına yaptığı harikalar için!
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
Yüceltsinler O'nu halk topluluğunda, Övgüler sunsunlar ileri gelenlerin toplantısında.
33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu, akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
Irmakları çöle çevirir, Pınarları kurak toprağa,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere, chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
Verimli toprağı çorak alana, Orada yaşayanların kötülüğü yüzünden.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
Çölü su birikintisine çevirir, Kuru toprağı pınara.
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako, ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
Açları yerleştirir oraya; Oturacak bir kent kursunlar,
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa ndipo anakolola zipatso zochuluka;
Tarlalar ekip bağlar diksinler, Bol ürün alsınlar diye.
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri, ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
RAB'bin kutsamasıyla, Çoğaldılar alabildiğine, Eksiltmedi hayvanlarını.
39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
Sonra azaldılar, alçaldılar, Baskı, sıkıntı ve acı yüzünden.
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
RAB rezalet saçtı soylular üzerine, Yolu izi belirsiz bir çölde dolaştırdı onları.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo ngati magulu a nkhosa.
Ama yoksulu sefaletten kurtardı, Davar sürüsü gibi çoğalttı ailelerini.
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala, koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
Doğru insanlar görüp sevinecek, Kötülerse ağzını kapayacak.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Aklı olan bunları göz önünde tutsun, RAB'bin sevgisini dikkate alsın.