< Masalimo 107 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Halleluja! Lov Herren, thi han er god, thi hans Miskundhed varer evindelig!
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
Så skal HERRENs genløste sige, de, han løste af Fjendens Hånd
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko, kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
og samlede ind fra Landene, fra Øst og Vest, fra Nord og fra Havet.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu, osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
I den øde Ørk for de vild, fandt ikke Vej til beboet By,
5 Iwo anamva njala ndi ludzu, ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
de led både Sult og Tørst, deres Sjæl var ved at vansmægte;
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
men de råbte til HERREN i Nøden, han frelste dem at deres Trængsler
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
og førte dem ad rette Vej, så de kom til beboet By.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
Lad dem takke HERREN for hans Miskundhed, for hans Underværker mod Menneskens Børn.
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
Thi han mættede den vansmægtende Sjæl og fyldte den sultne med godt.
10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu, amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
De sad i Mulm og Mørke, bundne i pine og Jern,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
fordi de havde stået Guds Ord imod og ringeagtet den Højestes Råd.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga; anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
Deres Hjerte var knuget af Kummer, de faldt, der var ingen, som hjalp;
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
men de råbte til HERREN i Nøden, han frelste dem af deres Trængsler,
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu ndipo anadula maunyolo awo.
førte dem ud af Mørket og Mulmet og sønderrev deres Bånd.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
Lad dem takke HERREN for hans Miskundhed, for hans Underværker mod Menneskens Børn.
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
Thi han sprængte Døre af Kobber og sønderslog Slåer af Jern.
17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira, ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
De sygnede hen for Synd og led for Brødes Skyld,
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
de væmmedes ved al Slags Mad, de kom Dødens Porte nær
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
men de råbte til Herren i Nøden, han frelste dem af deres Trængsler,
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa; anawalanditsa ku manda.
sendte sit Ord og lægede dem og frelste deres Liv fra Graven.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Lad dem takke HERREN for hans Miskundhed, for hans Underværker mod Menneskens Børn
22 Apereke nsembe yachiyamiko ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
og ofre Lovprisningsofre og med Jubel forkynnde hans Gerninger.
23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi; Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
De for ud på Havet i Skibe, drev Handel på vældige Vande,
24 Anaona ntchito za Yehova, machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
blev Vidne til HERRENs Gerninger, hans Underværker i Dybet;
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho imene inabweretsa mafunde ataliatali.
han bød, og et Stormvejr rejste sig, Bølgerne tårnedes op;
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya; pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
mod Himlen steg de, i Dybet sank de, i Ulykken svandt deres Mod;
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera; anali pa mapeto a moyo wawo.
de tumled og raved som drukne, borte var al deres Visdom;
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
men de råbte til HERREN i Nøden, han frelste dem af deres Trængsler,
29 Yehova analetsa namondwe, mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
skiftede Stormen til Stille, så Havets Bølger tav;
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata, ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
og glade blev de, fordi det stilned; han førte dem til Havnen, de søgte.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Lad dem takke HERREN for hans Miskundhed, for hans Underværker mod Menneskens Børn,
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
ophøje ham i Folkets Forsamling og prise ham i de Ældstes Kreds!
33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu, akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
Floder gør han til Ørken og Kilder til øde Land,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere, chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
til Saltsteppe frugtbart Land for Ondskabens Skyld hos dem, som - bor der.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
Ørken gør han til Vanddrag, det tørre Land til Kilder;
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako, ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
der lader han sultne bo, så de grunder en By at bo i,
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa ndipo anakolola zipatso zochuluka;
tilsår Marker og planter Vin og høster Afgrødens Frugt.
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri, ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
Han velsigner dem, de bliver mange, han lader det ikke skorte på Kvæg.
39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
De bliver få og segner under Modgangs og Kummers Tryk,
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
han udøser Hån over Fyrster og lader dem rave i vejløst Øde.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo ngati magulu a nkhosa.
Men han løfter den fattige op af hans Nød og gør deres Slægter som Hjorde;
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala, koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
de oprigtige ser det og glædes, men al Ondskab lukker sin Mund.
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Hvo som er viis, han mærke sig det og lægge sig HERRENs Nåde på Sinde!