< Masalimo 107 >
1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Hvalite Jahvu jer je dobar, jer je dovijeka ljubav njegova!
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
Tako nek' reknu svi otkupljenici koje Jahve otkupi iz ruke dušmanske
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko, kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
i koje skupi iz svih zemalja, s istoka i sa zapada, sa sjevera i s juga.
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu, osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
Lutahu pustinjom, u samoći pustoj, puta ne nalazeć' do naseljena grada.
5 Iwo anamva njala ndi ludzu, ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
Gladni su bili, žeđu izmoreni, duša je klonula u njima.
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
Tada zavapiše Jahvi u svojoj tjeskobi, i on ih istrže iz svih nevolja.
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
Pravim ih putem pÓovede da stignu ka gradu naseljenu.
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
Neka hvale Jahvu za dobrotu njegovu, za čudesa njegova sinovima ljudskim!
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
Jer gladnu dušu on nasiti, dušu izgladnjelu on napuni dobrima.
10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu, amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
U mraku sjeđahu i u tmini, sputani bijedom i gvožđima,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
jer su prkosili besjedama Božjim i prezreli naum Svevišnjega.
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga; anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
Srce im stoga skrši patnjama: posrtahu, a ne bješe nikog da im pomogne.
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
Tada zavapiše Jahvi u svojoj tjeskobi i on ih istrže iz svih nevolja.
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu ndipo anadula maunyolo awo.
Izvede ih iz tmina i mraka, raskide okove njihove.
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
Neka hvale Jahvu za dobrotu njegovu, za čudesa njegova sinovima ljudskim!
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
Jer razbi vrata mjedena i gvozdene polomi zasune.
17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira, ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
Zbog svojih bezakonja bolovahu oni, ispaštajuć' svoje opačine:
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
svako se jelo gadilo duši njihovoj, do vrata smrti oni dođoše.
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
Tada zavapiše Jahvi u svojoj tjeskobi i on ih istrže iz svih nevolja.
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa; anawalanditsa ku manda.
Riječ svoju posla da ih ozdravi i život im spasi od jame grobne.
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Neka hvale Jahvu za dobrotu njegovu, za čudesa njegova sinovima ljudskim!
22 Apereke nsembe yachiyamiko ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
Nek' prinose žrtve zahvalnice i kličući nek' djela njegova kazuju!
23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi; Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
Oni koji lađama zaploviše morem da po vodama silnim trguju:
24 Anaona ntchito za Yehova, machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
oni vidješe djela Jahvina, čudesa njegova na pučini.
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho imene inabweretsa mafunde ataliatali.
On reče i olujni se vjetar uzvitla što u visinu diže valove mora.
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya; pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
Do neba se dizahu, u bezdan se spuštahu, u nevolji duša im ginula.
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera; anali pa mapeto a moyo wawo.
Teturahu i posrtahu kao pijani, sva ih je mudrost izdala.
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
Tada zavapiše Jahvi u svojoj tjeskobi i on ih istrže iz svih nevolja.
29 Yehova analetsa namondwe, mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
Smiri oluju u tih povjetarac, valovi morski umukoše.
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata, ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
Obradovaše se tišini, u željenu luku on ih povede.
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
Neka hvale Jahvu za dobrotu njegovu, za čudesa njegova sinovima ljudskim!
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
Neka ga uzvisuju u narodnom zboru, neka ga hvale u vijeću staraca!
33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu, akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
On pretvori rijeke u pustinju, a izvore vodene u žednu zemlju;
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere, chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
plodonosnu zemlju u slanu pustaru zbog zloće žitelja njezinih.
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
On obrati pustinju u jezero, a zemlju suhu u vodene izvore
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako, ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
i naseli ondje izgladnjele te podigoše grad gdje će živjeti.
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa ndipo anakolola zipatso zochuluka;
Zasijaše njive, posadiše vinograde što im doniješe obilnu ljetinu.
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri, ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
I on ih blagoslovi te se namnožiše silno i stada im se ne smanjiše.
39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
Prorijeđeni bjehu i prezreni pod teretom patnja i nevolja.
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
Onaj što izlijeva prezir na knezove pusti ih da po bespuću pustom lutaju.
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo ngati magulu a nkhosa.
Iz nevolje pÓodiže ubogog i obitelji k'o stada ÓumnožÄi.
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala, koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
Videć' to, čestiti neka se raduju, a zloća neka sebi usta začepi!
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
Tko je mudar nek' o svemu tom razmišlja i nek' uvidi dobrotu Jahvinu!