< Masalimo 107 >

1 Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
請您們向上主讚頌,因為祂是美善寬仁,祂的仁慈永遠常存。
2 Owomboledwa a Yehova anene zimenezi amene Iyeyo anawawombola mʼdzanja la mdani,
歌詠此曲的人們是:上主親身所救贖的,由敵人手中救出的,
3 iwo amene anawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko, kuchokera kumadzulo ndi kummawa, kuchokera kumpoto ndi kummwera.
從各地召集來的,東南西北聚來的。
4 Ena anayendayenda mʼchipululu mopanda kanthu, osapeza njira yopitira ku mzinda kumene akanakakhazikikako.
他們在曠野和沙漠中漂流,找不到安居之城的道路。
5 Iwo anamva njala ndi ludzu, ndipo miyoyo yawo inafowokeratu.
他們口渴而又腹饑,生命已經奄奄一息;
6 Pamenepo analirira Yehova mʼmavuto awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
他們於急難中一哀救上主,上主即拯救他們脫離困苦,
7 Iye anawatsogolera mʼnjira yowongoka kupita ku mzinda umene anakakhazikikako.
引領他們走入正道,走內入可安居的城廓。
8 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi chifukwa cha machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
願他們感謝上主的仁慈,稱頌祂給人子顯的奇蹟。
9 pakuti Iye wapha ludzu la munthu womva ludzu ndipo wakhutitsa wanjala ndi zinthu zabwino.
因為祂使饑渴的人得到飽飫,祂使肚餓人享盡美物。
10 Ena anakhala mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu, amʼndende ovutika mʼmaunyolo achitsulo,
他們坐在黑暗與死影裏,盡為痛苦與鐵鍊所縛繫,
11 pakuti iwowo anawukira mawu a Mulungu ndi kunyoza uphungu wa Wammwambamwamba.
因為背棄了天主的命令,又輕視了至高者的叮嚀。
12 Kotero Iye anawapereka kuti agwire ntchito yakalavulagaga; anagwa pansi ndipo panalibe woti awathandize.
因此,祂以苦難折磨了他們的心神,他們跌倒了,卻沒有人來扶持他們。
13 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awo.
他們在急難中哀求上主,上主即救他們脫離困苦,
14 Yehova anawatulutsa mu mdima ndi mʼchisoni chachikulu ndipo anadula maunyolo awo.
領他們擺脫死影與黑暗,把他們的銬鐐完全弄斷。
15 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu onse,
願他們感謝上主的仁慈,稱頌祂給人子顯的奇蹟。
16 pakuti Iye amathyola zipata zamkuwa ndi kudula pakati mipiringidzo yachitsulo.
因為祂把銅門摧毀,又把鐵閂擊碎。
17 Ena anakhala zitsiru chifukwa cha njira zawo zowukira, ndipo anamva zowawa chifukwa cha mphulupulu zawo.
他們因行為邪惡而病重,因犯罪而遭受苦痛;
18 Iwo ananyansidwa ndi chakudya chilichonse ndipo anafika pafupi ndi zipata za imfa.
他們厭棄各樣的食物,快已接近死亡的門戶。
19 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iye anawapulumutsa ku masautso awowo.
他們於急難中一哀求主,上主即拯救他們脫離困苦。
20 Iye anatumiza mawu ake ndi kuwachiritsa; anawalanditsa ku manda.
主發一言就將他們病除,且拯救他們脫離了陰府。
21 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
願他們感謝上主[的仁慈,稱頌祂給人子顯的奇蹟。
22 Apereke nsembe yachiyamiko ndi kufotokoza za ntchito zake ndi nyimbo zachimwemwe.
願他們獻上感恩的祭獻,將祂的工程歡樂地宣傳。
23 Ena anayenda pa nyanja mʼsitima zapamadzi; Iwo anali anthu amalonda pa nyanja yayikulu.
他們乖船,下海行航,在大洋中往來經商,
24 Anaona ntchito za Yehova, machitidwe ake odabwitsa mʼnyanja yakuya.
他們看見過上主的奇異作為,遇到過祂行於汪洋中的奇跡:
25 Pakuti Iye anayankhula ndi kuwutsa mphepo yamkuntho imene inabweretsa mafunde ataliatali.
祂一發命,風浪狂掀,海中波檮頓時高翻,
26 Sitima za pamadzizo zinatukulidwa mmwamba ndi kutsikira pansi pakuya; pamene amawonongeka, kulimba mtima kwawo kunasungunuka.
時而忽躍沖天,時而忽墜棎淵;此危急之中,他們膽戰心寒,
27 Anachita chizungulire ndi kudzandira ngati anthu oledzera; anali pa mapeto a moyo wawo.
恍惚且暈眩,有如醉漢;一切的經驗全部紊亂。
28 Pamenepo analirira Yehova mʼmasautso awo ndipo Iyeyo anawapulumutsa ku masautso awo.
他們於急難中一哀求上主,上主即拯救他們脫離困苦。
29 Yehova analetsa namondwe, mafunde a mʼnyanja anatontholetsedwa.
祂化風暴為平靜,海濤頓時便安定;
30 Anali osangalala pamene kunakhala bata, ndipo Iye anawatsogolera ku dooko limene amalifuna.
祂使風平浪靜,大家個個歡忭,祂領他們登上了渴薶的海岸。
31 Ayamike Yehova chifukwa cha chikondi chake chosatha ndi machitidwe ake odabwitsa kwa anthu.
願他們感謝上主的仁慈,稱頌祂給人子的奇蹟,
32 Akuze Iye mu msonkhano wa anthu ndi kumutamanda pabwalo la akuluakulu.
在人民的集會中頌揚祂,在長老的議上讚美祂。
33 Iye anasandutsa mitsinje kukhala chipululu, akasupe otuluka madzi kukhala nthaka yowuma,
上主使河域變為荒灘,青使清水泉變成乾川,
34 ndiponso nthaka yachonde kukhala nthaka yamchere, chifukwa cha kuyipa kwa amene amakhala kumeneko.
使肥沃土地變為鹹田,都因當地居民的罪愆。
35 Anasandutsa chipululu kukhala mayiwe a madzi ndi nthaka yowuma kukhala akasupe a madzi oyenda;
祂又能使沙漠變成水源,使旱地變成水泉。
36 kumeneko Iye anabweretsa anthu anjala kuti azikhalako, ndipo iwo anamanga mzinda woti akhazikikeko.
把饑餓的人徒置在那地,使他們與興建者安居的城邑;
37 Anafesa mbewu mʼminda ndi kudzala mipesa ndipo anakolola zipatso zochuluka;
耕田種地,開懇了葡萄園,因此收穫果實,豐富出產。
38 Yehova anawadalitsa, ndipo chiwerengero chawo chinachuluka kwambiri, ndipo Iye sanalole kuti ziweto zawo zithe.
上主祝福了他們人口繁衍,賞賜他們的牲畜有增無減。
39 Kenaka chiwerengero chawo chinachepa ndipo iwo anatsitsidwa chifukwa cha mazunzo, mavuto ndi chisoni;
其後因慘遭災患苦茌難,人口減少而被棄如前。
40 Iye amene amakhuthulira mʼnyozo pa olemekezeka anawachititsa kuyendayenda mʼmalo owumawo wopanda njira.
但上主卻使權貴遭受恥辱,任他們徘徊歧途無路可走。
41 Koma Iyeyo anakweza anthu osowa kuchoka ku masautso awo ngati magulu a nkhosa.
但拯救貧窮人脫離災難,使他們家屬多如羊群一般。
42 Anthu olungama mtima amaona ndi kusangalala, koma anthu onse oyipa amatseka pakamwa pawo.
正直的人見到必然歡忭,但邪惡的人卻啞口無言。
43 Aliyense wanzeru asamalitse zinthu zimenezi ndi kuganizira za chikondi chachikulu cha Yehova.
那一位賢哲詳察此事,並能體會上主的仁慈!

< Masalimo 107 >