< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Halleluja. Tacker Herranom, ty han är mild, och hans godhet varar i evighet.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Ho kan uttala Herrans dråpeliga gerningar? och prisa all hans lofliga verk?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Salige äro de som budet hålla, och göra alltid rätt.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Herre, tänk på mig efter den nåd, som du dino folke lofvat hafver; bevisa oss dina hjelp;
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Att vi måge se dina utkorades välfärd, och glädja oss att dino folke väl går, och berömma oss med dinom arfvedel.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Vi hafve syndat med våra fäder; vi hafve misshandlat, och hafve ogudaktige varit.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Våre fäder uti Egypten ville icke förstå din under; de tänkte icke på dina stora godhet, och voro ohörige vid hafvet, nämliga röda hafvet.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Men han halp dem för sitt Namns skull, så att han sina magt beviste.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Och han näpste röda hafvet, och det vardt torrt; och förde dem genom djupen, såsom genom ena öken;
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Och halp dem ifrå deras hand, som dem hatade, och förlossade dem ifrå fiendans hand.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
Och vattnet fördränkte deras fiendar, så att icke en qvar blef.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Då trodde de uppå hans ord, och söngo hans lof.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Men de förgåto snarliga hans gerningar, och bidde intet efter hans råd.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Och de fingo lusta i öknene, och försökte Gud uti ödemarkene.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Men han gaf dem deras bön, och sände dem nog, tilldess dem vämjade dervid.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Och de satte sig upp emot Mose i lägrena; emot Aaron, Herrans heliga.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Jorden öppnade sig, och uppsvalg Dathan, och öfvertäckte Abirams rota.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Och eld vardt ibland deras rota upptänd; lågen uppbrände de ogudaktiga.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
De gjorde en kalf i Horeb, och tillbådo det gjutna belätet;
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Och förvandlade sina äro uti ens oxas liknelse, den gräs äter.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
De förgåto Gud sin Frälsare, som så stor ting uti Egypten gjort hade;
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Vidunder i Hams land, och förskräckeliga gerningar i röda hafvet.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Och han sade, att han ville förgöra dem, om Mose hans utkorade den plågan icke förtagit hade, och afvändt hans grymhet, att han icke platt skulle förderfva dem.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Och de föraktade det lustiga landet; de trodde icke hans ordom;
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Och knorrade i deras hyddom; de lydde intet Herrans röst.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Och han hof upp sina hand emot dem, att han skulle nederslå dem i öknene;
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
Och kasta deras säd ibland Hedningarna, och förströ dem i landen.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Och de gåfvo sig till BaalPeor, och åto af de döda afgudars offer;
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Och förtörnade honom med sin verk; då kom ock en plåga ibland dem.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Då trädde Pinehas fram, och förlikte sakena, och plågan vände åter.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Och det vardt honom räknadt till rättfärdighet, ifrå slägte till slägte, i evig tid.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Och de förtörnade honom vid trätovattnet; och de plågade Mose illa.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Ty de bedröfvade honom hans hjerta, så att någor ord undföllo honom.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
De förgjorde ock icke de folk, som dock Herren dem budit hade;
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Utan de blandade sig ibland Hedningarna, och lärde deras verk;
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Och tjente deras afgudom; de kommo dem på förargelse.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Och de offrade sina söner, och sina döttrar djeflom;
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Och utgöto oskyldigt blod, sina söners och döttrars blod, som de offrade Canaans afgudom; så att landet med blodskulder besmittadt vardt;
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Och orenade sig med sinom gerningom, och hor bedrefvo med sin verk.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Då förgrymmade sig Herrans vrede öfver sitt folk, och han fick en styggelse till sitt arf;
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Och gaf dem uti Hedningars händer; så att öfver dem rådde de som dem hätske voro.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Och deras fiender plågade dem, och de vordo kufvade under deras händer.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Han förlossade dem ofta; men de förtörnade honom med sin verk, och vordo få för deras missgerningars skull.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Och han såg till deras nöd, då han deras klagan hörde;
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Och tänkte på sitt förbund, som han med dem gjort hade; och det ångrade honom efter hans stora godhet;
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Och lät dem komma till barmhertighet, för allom dem som dem fångat hade.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Hjelp oss, Herre vår Gud, och för oss tillhopa ut ifrå Hedningarna; att vi måge tacka ditt helga Namn, och begå ditt lof.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Lofvad vare Herren, Israels Gud, ifrån evighet i evighet; och allt folk säga: Amen. Halleluja.

< Masalimo 106 >