< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Dejen que el Señor sea alabado. Alaben al Señor, porque él es bueno; porque su misericordia es inmutable para siempre.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
¿Quién puede dar cuenta de los grandes actos del Señor, o dejar en claro toda su alabanza?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Felices son aquellos cuyas decisiones son rectas, y el que hace justicia todo el tiempo.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Recuerda, oh Señor, cuando eres bueno con tu pueblo; Oh, deja que tu salvación venga a mí;
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Para que pueda ver el bienestar de las personas de tu elección y participe en la alegría de tu nación y enorgullezca de tu herencia.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Somos pecadores como nuestros padres, hemos hecho mal, nuestros actos son malos.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Nuestros padres no pensaron en tus maravillas en Egipto; ellos no guardaron en la memoria la gran cantidad de tus misericordias, sino que te dieron motivos para la ira en el mar, incluso en el Mar Rojo.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Pero él era su salvador a causa de su nombre, para que los hombres pudieran ver su gran poder.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Por su palabra, el mar Rojo se secó, y él los llevó por las aguas profundas como a través del desierto.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Y los tomó a salvo de las manos de sus enemigos, y los mantuvo lejos de los ataques de los que estaban contra ellos.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
Y las aguas pasaron sobre sus enemigos; todos ellos llegaron a su fin.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Entonces tuvieron fe en su palabra; ellos le dieron canciones de alabanza.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Pero el recuerdo de sus obras fue breve; no esperando ser guiado por él,
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Ellos dieron paso a sus malos deseos en la tierra baldía, y pusieron a Dios a prueba en el desierto.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Y él les dio su pedido, pero envió una enfermedad devastadora en sus almas.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Estaban llenos de envidia contra Moisés en las tiendas, y contra Aarón, el santo del Señor.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
La apertura de la tierra puso fin a Datán, cubriendo a Abiram y su banda.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Y se encendió un fuego entre sus tiendas; los pecadores fueron quemados por las llamas.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Hicieron un becerro en Horeb, y adoraron a una imagen de oro.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Y su gloria fue transformada en imagen de buey, cuyo alimento es hierba.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
No tenían memoria de Dios su salvador, que había hecho grandes cosas en Egipto;
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Obras de maravilla en la tierra de Ham, y cosas de miedo en el Mar Rojo.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Y él se proponía poner fin a ellos si Moisés, su siervo especial, no se hubiera levantado delante de él, entre él y su pueblo, haciendo retroceder su ira, para guardarlos de la destrucción.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Estaban disgustados con la buena tierra; no tenían fe en su palabra;
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Hablando contra él secretamente en sus tiendas, no escucharon la voz del Señor.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Entonces les juró que los exterminaría en la tierra baldía.
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
para que sus hijos se mezclen entre las naciones, y sean enviados a otras tierras.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Y se juntaron con Baal-peor, y tomaron parte en las ofrendas a los muertos.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Entonces lo enojaron por su comportamiento; y él envió enfermedad sobre ellos.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Entonces se levantó Finees y oró por ellos; y la enfermedad no se expandió.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Y todas las generaciones que vinieron después de él guardaban para siempre el recuerdo de su justicia.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
E hicieron enojar a Dios otra vez en las aguas de Meriba, y Moisés se angustió por causa de ellos;
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Porque ellos hicieron amargar su espíritu, y él dijo cosas impías.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
No pusieron fin a los pueblos, como el Señor había dicho;
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Pero se unieron a las naciones, aprendiendo sus obras.
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Y adoraron a las imágenes; que eran un peligro para ellos:
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Incluso hicieron ofrendas de sus hijos y sus hijas a espíritus malignos,
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Y dieron la sangre de sus hijos y de sus hijas que no habían hecho mal, ofreciéndolas a las imágenes de Canaán; y la tierra quedó contaminada con sangre.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Y se contaminaron con sus obras, yendo tras sus malos deseos.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Entonces la ira del Señor ardió contra su pueblo, y él se enojó contra su heredad.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Y él los entregó en manos de las naciones; y fueron gobernados por sus enemigos.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Por ellos fueron aplastados, y humillados bajo sus manos.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Una y otra vez los hizo libres; pero sus corazones se volvieron contra su propósito, y fueron vencidos por sus pecados.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Pero cuando su clamor llegó a sus oídos, tuvo piedad de su problema:
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Y tuvo en cuenta su acuerdo con ellos, y en su gran misericordia les dio el perdón.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Él puso lástima en los corazones de aquellos que los hicieron prisioneros.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Sé nuestro Salvador, Señor Dios nuestro, y nos volvamos a reunir de entre las naciones, para que glorifiquemos tu santo nombre y nos gloriamos en tu alabanza.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Alabado sea el Señor Dios de Israel por los siglos de los siglos; y que toda la gente diga: que así sea. Alaba al Señor.

< Masalimo 106 >