< Masalimo 106 >
1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
¡Aleluya! Den gracias a Yavé, Porque Él es bueno, Porque para siempre es su misericordia.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
¿Quién puede contar las proezas de Yavé? ¿Quién proclama toda su alabanza?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
¡Dichosos los que guardan recto juicio, Los que practican justicia en todo tiempo!
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Acuérdate de mí, oh Yavé, Según tu buena voluntad para tu pueblo. Visítame con tu salvación,
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Para que yo vea el bien de tus escogidos, Para que me regocije por la alegría de tu pueblo, Que me gloríe con tu heredad.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Como nuestros antepasados pecamos. Cometimos iniquidad. Nos portamos perversamente.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Nuestros antepasados no entendieron tus maravillas en Egipto. No recordaron tus numerosas bondades, Sino se rebelaron junto al mar, en el mar Rojo.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Pero Él los salvó por amor a su Nombre Para que fuera evidente su poder.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Reprendió al mar Rojo Y lo secó, Y los condujo por las profundidades, Como por un desierto.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Así los salvó de [la] mano del que [los] odiaba, Y los redimió de la mano del enemigo.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
Cubrieron las aguas a sus adversarios, No quedó ni uno de ellos.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Entonces creyeron a sus Palabras, Y cantaron su alabanza.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Muy pronto olvidaron sus obras. No esperaron su consejo.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Con avidez desearon comer en el desierto, Y en lugar despoblado tentaron a ʼElohim.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Él les dio lo que pidieron, Pero envió mortandad sobre ellos.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Tuvieron envidia de Moisés en el campamento, Y de Aarón, el consagrado a Yavé.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Se abrió la tierra Y se tragó a Datán, Y cubrió al grupo de Abiram.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Un fuego se encendió contra su grupo. La llama devoró a los perversos.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Hicieron un becerro en Horeb. Se postraron ante una imagen de fundición.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Así cambiaron la Gloria de ellos Por la imagen de un becerro que come hierba.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Olvidaron al ʼEL, su Salvador, Quien hizo grandes cosas en Egipto,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Maravillas en la tierra de Cam, Portentos en el mar Rojo.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Por tanto Él dijo que los destruiría. Si no fuera porque Moisés su escogido, Se puso en la brecha delante de Él Con la intención de que no los destruyera.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Luego despreciaron [la] tierra deseable. No creyeron en la Palabra de Él,
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Sino murmuraron en sus tiendas. No escucharon la voz de Yavé.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Por tanto les juró Que caerían en el desierto,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
Que dispersaría su descendencia entre las naciones Y los esparciría por las tierras.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Se unieron también a Baal-peor Y comieron lo sacrificado a los muertos.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Así [lo] provocaron a ira con sus obras, Y una mortandad irrumpió entre ellos.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Pero Finees se levantó e intervino, Y la mortandad se detuvo,
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Y le fue atribuido como justicia Por todas las generaciones para siempre.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
También [lo] provocaron a ira en las aguas de Meriba, Y salió mal Moisés por causa de ellos,
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Porque hicieron rebelar su espíritu, Y él habló precipitadamente con sus labios.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
No destruyeron a los pueblos, Como Yavé les mandó,
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Sino se mezclaron con gentiles. Aprendieron sus prácticas,
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Y sirvieron a sus ídolos, Los cuales fueron una trampa.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Sacrificaron sus hijos y sus hijas a los demonios
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Y derramaron sangre inocente, La sangre de sus hijos y de sus hijas, A quienes sacrificaron a los ídolos de Canaán, Y la tierra fue contaminada con la sangre.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Así se contaminaron con las prácticas de ellos, Y se prostituyeron con sus hechos.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Por tanto la ira de Yavé se encendió contra su pueblo, Y Él repugnó su heredad.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Los entregó en [la] mano de los gentiles, Y aquellos que los odiaban gobernaron sobre ellos.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Sus enemigos también los oprimieron, Y fueron sometidos bajo su poder.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Muchas veces los libró, Pero ellos se rebelaron contra su consejo en su designio, Y así se hundieron en su iniquidad.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Sin embargo, Él miraba su angustia Y escuchaba su clamor.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Recordaba su Pacto por amor a ellos, Y se compadecía según la grandeza de su misericordia.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
También promovió que fueran [objeto] de misericordia Por parte de todos los que los tenían cautivos.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Oh Yavé, ʼElohim nuestro, sálvanos. Recógenos de entre las naciones, Para que demos gracias a tu santo Nombre Y nos gloriemos en tus alabanzas.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
¡Bendito sea Yavé, el ʼElohim de Israel, Desde la eternidad hasta la eternidad! Y todo el pueblo diga: ¡Amén! ¡Aleluya!