< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
¡Alaben al Señor! ¡Agradézcanle, porque es bueno! Su gran amor durará para siempre.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
¿Quién puede dar cuenta de todas las maravillas que el Señor ha hecho? ¿Quién puede darle toda la alabanza que merece?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Felices son esos que tratan a la gente de forma justa, quienes siempre hacen lo correcto.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Acuérdate de mi, por favor, cuando seas generoso con tu pueblo; piensa en mí cuando vengas a salvar.
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Déjame ver a tu pueblo escogido prosperar; déjame alegrarme juntamente con tu nación santa; déjame compartir tu gozo con los tuyos.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Hemos pecado como nuestros antepasados. Nos hemos equivocado. Somos culpables.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
No prestaron atención a todas las cosas buenas que hiciste. No guardaron en su corazón cuánto los amabas, sino que eligieron rebelarse en el mar Rojo.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Tanto así que los salvó por su carácter santo, y para mostrar su poder
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Él dio la orden al mar Rojo, y este se secó. Guió a su pueblo a través de la profundidad del mar como si fueran por el desierto.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Los rescató de aquellos que lo odiaban; los salvó del poder de sus enemigos.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
El agua ahogó a sus enemigos, ni uno de ellos sobrevivió,
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Entonces su pueblo confió en lo que él había prometido, y cantó alabanzas a su nombre.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Pero ellos olvidaron rápidamente lo que Dios había hecho por ellos, y no escucharon sus advertencias.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Estaban llenos de ansias desesperadas en el desierto; provocaron a Dios en el desierto.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Dios les dio lo que querían, pero también les envió una plaga.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
La gente se volvió celosa de Moisés, y de Aarón, los sacerdotes santos del Señor.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
La tierra se abrió y se tragó a Datán; sepultó a Abiram y a sus seguidores.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Fuego ardiente se encendió en medio de ellos. Una llama que los quemó a todos.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
En el monte Sinaí elaboraron un becerro, se postraron ante un ídolo de metal.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
¡Reemplazaron su rey de gloria por un toro que comía yerba!
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Se olvidaron de Dios, su Salvador, quien había hecho cosas maravillosas en Egipto;
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
obrando toda clase de milagros en la tierra de Cam, haciendo cosas maravillosas en el mar Rojo.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Y entonces dijo que iba a destruirlos, pero Moisés, su líder escogido, se colocó entre Dios y el pueblo para persuadirlo de nos destruirlos en su ira.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Más tarde el pueblo se rehusó a entrar a la tierra prometida; no confiaron en que Él cumpliría lo que había prometido.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Hablaban en sus tiendas sobre el Señor, y se rehusaron a obedecer lo que les había ordenado.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Entonces levantó su mano para hacerles una seria advertencia de que los destruiría en el desierto,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
que dispersaría a sus descendientes entre las naciones, mandándolos a países lejanos.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Proclamaron fidelidad a Baal Peor, y comieron alimento sacrificado a los muertos.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Provocaron al Señor con lo que hicieron, haciéndolo enojar, y una plaga cayó sobre ellos.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Pero Finees tomó un lugar por el Señor e intervino, y la plaga se detuvo.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Ha sido considerado como un hombre que vivió con rectitud desde entonces hasta ahora, durante todas las generaciones.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
También hicieron airar al Señor en las aguas de Meribá, cuando las cosas se pusieron en contra de Moisés por culpa de ellos.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Lo hicieron enfurecer tanto que habló sin pensar en el calor del momento.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
No destruyeron a los pueblos paganos como el Señor les había dicho,
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
sino que en su lugar se unieron a ellos y adoptaron su estilo de vida.
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Adoraron a sus ídolos paganos que se convirtieron en una trampa para ellos.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Incluso rindieron en sacrificio a sus hijos e hijas a esos demonios.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Derramaron sangre de niños inocentes, sus propios hijos, sacrificándolos a los dioses de Canaán. Al hacerlo, mancharon la tierra con sangre.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Incluso mancharon sus propias vidas con lo que hicieron: sus acciones fueron adulterio espiritual.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Por eso el Señor se airó con su pueblo, odió a aquellos que le pertenecían.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Y los entregó a las naciones paganas. Estos pueblos que los odiaban ahora se convirtieron en sus dirigentes.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Sus enemigos los dominaron y los doblegaron con su poder.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
El Señor los rescató repetidas veces, pero ellos continuaron con sus actos rebeldes, hasta que fueron destruidos por sus propios pecados.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Pero, a pesar de todo esto, el Señor fue movido por su sufrimiento; oyó sus lamentos quejumbrosos.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Recordó el pacto que había hecho con ellos, y se contuvo por gran bondad y amor.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Hizo que los pueblos que los habían capturado los trataran con misericordia.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
¡Sálvanos, Señor, Dios nuestro! reúnenos nuevamente de entre todas las naciones, para que podamos agradecerte y hablar de lo maravilloso que eres.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
¡Cuán grande es el Señor, el Dios de Israel, quien vive por siempre y para siempre! ¡Todo el mundo diga “Amén”! ¡Alaben al Señor!

< Masalimo 106 >