< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Louvae ao Senhor. Louvae ao Senhor, porque elle é bom, porque a sua misericordia dura para sempre.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Quem pode referir as obras poderosas do Senhor? Quem annunciará os seus louvores?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Bemaventurados os que guardam o juizo, o que obra justiça em todos os tempos.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Lembra-te de mim, Senhor, segundo a tua boa vontade para com o teu povo: visita-me com a tua salvação;
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Para que eu veja os bens de teus escolhidos, para que eu me alegre com a alegria do teu povo, para que me glorie com a tua herança.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Nós peccámos com os nossos paes, commettemos a iniquidade, obrámos perversamente.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Nossos paes não entenderam as tuas maravilhas no Egypto; não se lembraram da multidão das tuas misericordias; antes o provocaram no mar, sim no Mar Vermelho.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Não obstante, elle os salvou por amor do seu nome, para fazer conhecido o seu poder.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Reprehendeu o Mar Vermelho e se seccou, e os fez caminhar pelos abysmos como pelo deserto.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
E os livrou da mão d'aquelle que os aborrecia, e os remiu da mão do inimigo.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
E as aguas cobriram os seus adversarios: nem um só d'elles ficou.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Então creram as suas palavras, e cantaram os seus louvores.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Porém cedo se esqueceram das suas obras; não esperaram o seu conselho,
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Mas deixaram-se levar da cubiça no deserto, e tentaram a Deus na solidão.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
E elle lhes cumpriu o seu desejo, mas enviou magreza ás suas almas.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
E invejaram a Moysés no campo, e a Aarão, o sancto do Senhor.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Abriu-se a terra, e enguliu a Dathan, e cobriu a gente de Abiram.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
E um fogo se accendeu na sua gente: a chamma abrazou os impios.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Fizeram um bezerro em Horeb, e adoraram a imagem fundida.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
E converteram a sua gloria na figura de um boi que come herva.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Esqueceram-se de Deus, seu salvador, que fizera grandezas no Egypto,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Maravilhas na terra de Cão, coisas tremendas no Mar Vermelho.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Pelo que disse que os destruiria, se Moysés, seu escolhido, se não pozesse perante elle na abertura, para desviar a sua indignação, afim de os não destruir.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Tambem desprezaram a terra aprazivel: não creram na sua palavra.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Antes murmuraram nas suas tendas, e não deram ouvidos á voz do Senhor.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Pelo que levantou a sua mão contra elles, para os derribar no deserto;
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
Para derribar tambem a sua semente entre as nações, e espalhal-os pelas terras.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Tambem se juntaram com Baal-peor, e começaram os sacrificios dos mortos.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Assim o provocaram á ira com as suas invenções; e a peste rebentou entre elles.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Então se levantou Phineas, e fez juizo, e cessou aquella peste.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
E isto lhe foi contado como justiça, de geração em geração, para sempre.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Indignaram-n'o tambem junto ás aguas da contenda, de sorte que succedeu mal a Moysés, por causa d'elles;
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Porque irritaram o seu espirito, de modo que fallou imprudentemente com seus labios.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Não destruiram os povos, como o Senhor lhes dissera.
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Antes se misturaram com as nações, e aprenderam as suas obras.
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
E serviram aos seus idolos, que vieram a ser-lhes um laço.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Demais d'isto, sacrificaram seus filhos e suas filhas aos demonios,
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
E derramaram sangue innocente, o sangue de seus filhos e de suas filhas, que sacrificaram aos idolos de Canaan; e a terra foi manchada com sangue.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Assim se contaminaram com as suas obras, e se prostituiram com os seus feitos.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Pelo que se accendeu a ira do Senhor contra o seu povo, de modo que abominou a sua herança.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
E os entregou nas mãos das nações; e aquelles que os aborreciam se assenhorearam d'elles.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
E os seus inimigos os opprimiram, e foram humilhados debaixo das suas mãos.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Muitas vezes os livrou, mas o provocaram com o seu conselho, e foram abatidos pela sua iniquidade.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Comtudo, attendeu á sua afflicção, ouvindo o seu clamor.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
E se lembrou do seu concerto, e se arrependeu segundo a multidão das suas misericordias.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Pelo que fez com que d'elle tivessem misericordia os que os levaram captivos.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Salva-nos, Senhor, nosso Deus, e congrega-nos d'entre as nações, para que louvemos o teu nome sancto, e nos gloriemos no teu louvor.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Bemdito seja o Senhor, Deus d'Israel, de eternidade em eternidade, e todo o povo diga: Amen. Louvae ao Senhor.

< Masalimo 106 >