< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Halleluja. Wysławiajcie Pana; albowiem dobry, albowiem na wieki miłosierdzie jego.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Któż wysłowi niezmierną moc Pańską, a wypowie wszystkę chwałę jego?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Błogosławieni, którzy strzegą sądu, a czynią sprawiedliwość na każdy czas.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Pamiętaj na mię, Panie! dla miłości ku ludowi swemu; nawiedźże mię zbawieniem swojem,
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Abym używał dobrego z wybranymi twoimi, a weselił się w radości narodu twego, i chlubił się wespół z dziedzictwem twojem.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Zgrzeszyliśmy z ojcami swymi; niesprawiedliwieśmy czynili, i nieprawość popełniali.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Ojcowie nasi w Egipcie nie zrozumieli cudów twoich, ani pamiętali na wielkość miłosierdzia twego; ale odpornymi byli przy morzu Czerwonem.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
A wszakże ich wyswobodził dla imienia swego, aby oznajmił moc swoję.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Bo zgromił morze Czerwone, i wyschło, a przewiódł ich przez przepaści, jako przez puszczę.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
A tak zachował ich od ręki tego, który ich miał w nienawiści, a wykupił ich z ręki nieprzyjacielskiej.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
W tem okryły wody tych, którzy ich ciążyli; nie został ani jeden z nich.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
A choć uwierzyli słowom jego, i wysławiali chwałę jego:
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Przecież prędko zapomnieli na sprawy jego, i nie czekali na rady jego.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Ale zdjęci będąc chciwością na puszczy, kusili Boga na pustyniach.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
I dał im, czego żądali, a wszakże przepuścił suchoty na nich.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Zatem gdy się wzruszyli zawiścią przeciw Mojżeszowi w obozie, i przeciw Aaronowi, świętemu Pańskiemu:
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Otworzyła się ziemia, i pożarła Datana, i okryła rotę Abironową,
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
I zapalił się ogień na zebranie ich; płomień spalił niepobożnych.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Sprawili i cielca na Horebie, i kłaniali się bałwanowi litemu,
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
I odmienili chwałę swą w podobieństwo wołu, jedzącego trawę.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Zapomnieli na Boga, wybawiciela swego, który czynił wielkie rzeczy w Egipcie;
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Rzeczy dziwne w ziemi Chamowej, rzeczy straszne przy morzu Czerwonem.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Przetoż rzekł, że ich chciał wytracić, gdyby się był Mojżesz, wybrany jego, nie stawił w onem rozerwaniu przed nim, a nie odwrócił popędliwości jego, aby ich nie tracił.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Wzgardzili też ziemią pożądaną, nie wierząc słowu jego.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
I szemrząc w namiotach swoich, nie byli posłuszni głosowi Pańskiemu.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Przetoż podniósł rękę swoję przeciwko nim, aby ich pobił na puszczy;
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
A żeby rozrzucił nasienie ich między pogan, i rozproszył ich po ziemiach.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Sprzęgli się też byli z bałwanem Baalfegorem, a jedli ofiary umarłych.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
A tak draźnili Boga sprawami swemi, że się na nich oborzyła plaga;
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Aż się zastawił Finees, a pomstę uczynił, i rozerwana jest ona plaga;
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Co mu poczytano ku sprawiedliwości od narodu do narodu, aż na wieki.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Znowu go byli wzruszyli do gniewu u wód Meryba, tak, iż się źle działo i z Mojżeszem dla nich.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Albowiem rozdraźnili ducha jego, że wyrzekł co niesłuszne usty swemi.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Nadto nie wytracili onych narodów, o których im był Pan powiedział.
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Ale pomięszawszy się z onemi narodami, nauczyli się spraw ich:
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
I służyli bałwanom ich, które im były sidłem.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Albowiem dyjabłom ofiarowali synów swoich, i córki swoje,
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
I wylewali krew niewinną, krew synów swoich, i córek swoich, których ofiarowali bałwanom rytym Chananejskim, tak, że splugawiona była ziemia onem krwi rozlaniem.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
I zmazali się sprawami swemi, a cudzołożyli wynalazkami swemi.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Przetoż zapaliwszy się Pan w popędliwości przeciw ludowi swemu, obrzydził sobie dziedzictwo swoje,
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
I podał ich w ręce poganom; a panowali nad nimi, którzy ich mieli w nienawiści;
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
I uciskali ich nieprzyjaciele ich, tak, że poniżeni byli pod ręką ich.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Częstokroć ich wybawiał; wszakże go oni wzruszali do gniewu radami swemi, zaczem poniżeni byli dla nieprawości swoich.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
A wszakże wejrzał na ucisk ich, i usłyszał wołanie ich.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Bo sobie wspomniał na przymierze swoje z nimi, a żałował tego według wielkiej litości swojej.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Tak, że im zjednał miłosierdzie przed oczyma wszystkich, którzy ich byli pojmali.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Wybawże nas, Panie, Boże nasz! a zgromadź nas z tych pogan, abyśmy wysławiali imię świętobliwości twojej, a chlubili się w chwale twojej.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Błogosławiony Pan, Bóg Izraelski, od wieków aż na wieki; na co niech rzecze wszystek lud: Amen, Halleluja.

< Masalimo 106 >