< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Alleluja. Confitemini Domino, quoniam bonus, quoniam in sæculum misericordia ejus.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Quis loquetur potentias Domini; auditas faciet omnes laudes ejus?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Beati qui custodiunt judicium, et faciunt justitiam in omni tempore.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Memento nostri, Domine, in beneplacito populi tui; visita nos in salutari tuo:
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
ad videndum in bonitate electorum tuorum; ad lætandum in lætitia gentis tuæ: ut lauderis cum hæreditate tua.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Peccavimus cum patribus nostris: injuste egimus; iniquitatem fecimus.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Patres nostri in Ægypto non intellexerunt mirabilia tua; non fuerunt memores multitudinis misericordiæ tuæ. Et irritaverunt ascendentes in mare, mare Rubrum;
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
et salvavit eos propter nomen suum, ut notam faceret potentiam suam.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Et increpuit mare Rubrum et exsiccatum est, et deduxit eos in abyssis sicut in deserto.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Et salvavit eos de manu odientium, et redemit eos de manu inimici.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
Et operuit aqua tribulantes eos; unus ex eis non remansit.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Et crediderunt verbis ejus, et laudaverunt laudem ejus.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Cito fecerunt; obliti sunt operum ejus: et non sustinuerunt consilium ejus.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Et concupierunt concupiscentiam in deserto, et tentaverunt Deum in inaquoso.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Et dedit eis petitionem ipsorum, et misit saturitatem in animas eorum.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Et irritaverunt Moysen in castris; Aaron, sanctum Domini.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Aperta est terra, et deglutivit Dathan, et operuit super congregationem Abiron.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Et exarsit ignis in synagoga eorum: flamma combussit peccatores.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Et fecerunt vitulum in Horeb, et adoraverunt sculptile.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Et mutaverunt gloriam suam in similitudinem vituli comedentis fœnum.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Obliti sunt Deum qui salvavit eos; qui fecit magnalia in Ægypto,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
mirabilia in terra Cham, terribilia in mari Rubro.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Et dixit ut disperderet eos, si non Moyses, electus ejus, stetisset in confractione in conspectu ejus, ut averteret iram ejus, ne disperderet eos.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Et pro nihilo habuerunt terram desiderabilem; non crediderunt verbo ejus.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Et murmuraverunt in tabernaculis suis; non exaudierunt vocem Domini.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Et elevavit manum suam super eos ut prosterneret eos in deserto:
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
et ut dejiceret semen eorum in nationibus, et dispergeret eos in regionibus.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Et initiati sunt Beelphegor, et comederunt sacrificia mortuorum.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Et irritaverunt eum in adinventionibus suis, et multiplicata est in eis ruina.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Et stetit Phinees, et placavit, et cessavit quassatio.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Et reputatum est ei in justitiam, in generationem et generationem usque in sempiternum.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Et irritaverunt eum ad aquas contradictionis, et vexatus est Moyses propter eos:
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
quia exacerbaverunt spiritum ejus, et distinxit in labiis suis.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Non disperdiderunt gentes quas dixit Dominus illis:
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
et commisti sunt inter gentes, et didicerunt opera eorum;
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
et servierunt sculptilibus eorum, et factum est illis in scandalum.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Et immolaverunt filios suos et filias suas dæmoniis.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Et effuderunt sanguinem innocentem, sanguinem filiorum suorum et filiarum suarum, quas sacrificaverunt sculptilibus Chanaan. Et infecta est terra in sanguinibus,
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
et contaminata est in operibus eorum: et fornicati sunt in adinventionibus suis.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Et iratus est furore Dominus in populum suum, et abominatus est hæreditatem suam.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Et tradidit eos in manus gentium; et dominati sunt eorum qui oderunt eos.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Et tribulaverunt eos inimici eorum, et humiliati sunt sub manibus eorum;
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
sæpe liberavit eos. Ipsi autem exacerbaverunt eum in consilio suo, et humiliati sunt in iniquitatibus suis.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Et vidit cum tribularentur, et audivit orationem eorum.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Et memor fuit testamenti sui, et pœnituit eum secundum multitudinem misericordiæ suæ:
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
et dedit eos in misericordias, in conspectu omnium qui ceperant eos.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Salvos nos fac, Domine Deus noster, et congrega nos de nationibus: ut confiteamur nomini sancto tuo, et gloriemur in laude tua.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Benedictus Dominus Deus Israël, a sæculo et usque in sæculum; et dicet omnis populus: Fiat, fiat.

< Masalimo 106 >