< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Idaydayawyo ni Yahweh. Agyamankayo kenni Yahweh ta naimbag isuna, ta agtalinaed iti agnanayon ti kinapudnona iti tulagna.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Siasino ti makabael a mangbilang kadagiti mannakabalin nga aramid ni Yahweh wenno mangipakaammo a naan-anay kadagiti amin nga aramidna a rumbeng a bigbigen?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Nagasat dagiti agaramid iti maiparbeng, ken dagiti kanayon a nalinteg dagiti aramidda.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Lagipennak O Yahweh, inton ipakitam ti kinaimbagmo kadagiti tattaom; tulungannak inton isalakanmo ida.
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Ket makitakto ti panagdur-as dagiti pinilim, agrag-oak gapu iti kinaragsak ti nasionmo, ken agpasindayagak a kadua dagiti tawidmo.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Nagbasolkami a kas kadagiti kapuonanmi; nagbiddutkami ken nakaaramidkami iti dakes.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Saan a naragsakan dagiti ammami kadagiti nakaskasdaaw nga aramidmo idiay Egipto; saanda nga inkaskaso dagiti adu nga aramidmo kas panangipakitam iti kinapudnom iti tulagmo; nagsukirda iti kaaddada idiay baybay, ti baybay dagiti Runo.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Nupay kasta, insalakanna ida gapu iti naganna tapno maiparangarangna ti pannakabalinna.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Tinubngarna ti baybay dagiti Runo, ket namagaan daytoy. Ket indalanna ida iti kaadalman, a kas iti let-ang.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Insalakanna ida manipud iti ima dagiti nanggura kadakuada, ken inispalna ida manipud iti pannakabalin ti kabusor.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
Ngem linemmes dagiti dandanum dagiti kabusorda; awan ti uray maysa kadakuada iti nakalasat.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Ket namatida kadagiti sasaona, ken nagkantada iti pagdaydayaw kenkuana.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Ngem nalipatanda a dagus dagiti inaramidna; saanda nga inuray dagiti pagannurotanna.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Naaddaanda iti saan a makapnek a panagtarigagay iti makan idiay let-ang, ket sinuotda ti Dios idiay disierto.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Intedna kadakuada dagiti kiddawda, ngem nangibaon isuna iti sakit a nangparigat kadagiti bagida.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Idiay kampo, nagimonda ken Moises kenni Aaron a nasantoan a padi ni Yahweh.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Nagringngat ti daga ket inallun-onna ni Datan ken ginaburanna dagiti pasurot ni Abiram.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Rimsua ti apuy kadakuada; ket inuram ti apuy dagiti nadangkes.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Nagaramidda iti baka idiay Horeb ket nagrukbabda iti nahulma a landok nga imahe.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Insukatda ti dayag ti Dios iti imahe dagiti baka a magmangan iti ruot.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Nilipatanda ti Dios a Mangisalakanda, a nangaramid kadagiti nakaskasdaaw nga aramid idiay Egipto.
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Nangaramid isuna kadagiti nakaskasdaaw a banbanag idiay daga ni Ham ken naindaklan nga aramid idiay baybay dagiti Runo.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Ikeddengna koman ti pannakadadaelda, no saan a bimmallaet ni Moises a pinilina kenkuana idiay naggidiatan tapno pukawen ti ungetna a mangdadael kadakuada.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Ket inlaksidda ti nadam-eg a daga; saanda a pinati ti karina,
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
ngem nagtanabutobda kadagiti toldada, ket saanda a nagtulnog kenni Yahweh.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Isu nga ingngatona ti imana ken insapatana kadakuada nga itulokna a matayda idiay disierto,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
iwarasna dagiti kaputotanda kadagiti nasion, ken iwarasna ida kadagiti gangannaet a dagdaga.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Nagrukbabda iti Baal ti Peor ket kinnanda dagiti naidaton kadagiti natay.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Pinaungetda isuna gapu kadagiti tignayda, ket rimsua ti maysa a didigra kadakuada.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Ket timmakder ni Finees tapno mangiballaet, ket nagsardeng ti didigra.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Naibilang kenkuana daytoy a kas nalinteg nga aramid kadagiti amin a henerasion iti agnanayon.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Pinaungetda pay ni Yahweh idiay danum ti Meriba, ket nagsagaba ni Moises gapu kadakuada.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Pinagsakitda ti nakem ni Moises, ket nagsao isuna a siraranggas.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Saanda a dinadael dagiti nasion a kas imbilin ni Yahweh kadakuada,
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
ngem nakilangenlangenda kadagiti nasion ket nasursoroda dagiti wagas dagitoy
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
ken nagrukbabda kadagiti didiosen dagitoy a nasion, nga isu ti nagbalin a palab-og kadakuada.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Indatonda dagiti annakda kadagiti demonio.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Nangpasayasayda iti dara iti awan basolna, ti dara dagiti annakda a lallaki ken babbai, nga indatonda kadagiti didiosen ti Canaan, tinulawanda ti daga babaen iti dara.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Natulawanda babaen kadagiti aramidda; kasda la kadagiti balangkantis kadagiti tignayda.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Isu a nakaunget ni Yahweh kadagiti tattaona, ket linaksidna dagiti bukodna a tattao.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Inyawatna ida kadagiti nasion, ket inturayan ida dagiti nanggura kadakuada.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Indadanes ida dagiti kabusorda, ken naikabilda iti panangituray dagitoy.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Adu a daras nga immay isuna tapno tulonganna ida, ngem nagsukirda latta ket naipababada gapu iti bukodda a basol.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Nupay kasta, impangagna dagiti pakariribukanda idi immasugda kenkuana.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Linagipna ti tulagna kadakuada ket naasian isuna gapu iti kinapudnona iti tulagna.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Nagtignay isuna kadagiti nangparmek kadakuada tapno maasida kadakuada.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Isalakannakami O Yahweh a Diosmi. Ummongennakami manipud kadagiti nasion tapno makapagyamankami iti nasantoan a naganmo ken ipannakkelmi ti dayawmo.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Maidaydayaw koma ni Yahweh, ti Dios ti Israel iti agnanayon nga awan inggana. Kinuna amin dagiti tattao, “Amen.” Idaydayawyo ni Yahweh. Maikalima a Libro

< Masalimo 106 >