< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Halleluja! Danket dem HERRN; denn er ist freundlich, und seine Güte währet ewiglich.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Wer kann die großen Taten des HERRN ausreden und alle seine löblichen Werke preisen?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Wohl denen, die das Gebot halten und tun immerdar recht!
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
HERR, gedenke mein nach der Gnade, die du dem Volk verheißen hast; beweise uns deine Hilfe,
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
daß wir sehen mögen die Wohlfahrt deiner Auserwählten und uns freuen, daß es deinem Volk wohl geht, und uns rühmen mit deinem Erbteil.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Wir haben gesündigt samt unsern Vätern; wir haben mißgehandelt und sind gottlos gewesen.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Unsre Väter in Ägypten wollten deine Wunder nicht verstehen; sie gedachten nicht an deine große Güte und waren ungehorsam am Meer, am Schilfmeer.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Er half ihnen aber um seines Namens willen, daß er seine Macht bewiese.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Und er schalt das Schilfmeer: da ward's trocken, und führte sie durch die Tiefen wie in einer Wüste
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
und half ihnen von der Hand des, der sie haßte, und erlöste sie von der Hand des Feindes;
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
und die Wasser ersäuften ihre Widersacher, daß nicht einer übrig blieb.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Da glaubten sie an seine Worte und sangen sein Lob.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Aber sie vergaßen bald seiner Werke; sie warteten nicht auf seinen Rat.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Und sie wurden lüstern in der Wüste und versuchten Gott in der Einöde.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Er aber gab ihnen ihre Bitte und sandte ihnen genug, bis ihnen davor ekelte.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Und sie empörten sich wider Mose im Lager, wider Aaron, den Heiligen des HERRN.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Die Erde tat sich auf und verschlang Dathan und deckte zu die Rotte Abirams,
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
und Feuer ward unter ihrer Rotte angezündet, die Flamme verbrannte die Gottlosen.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Sie machten ein Kalb am Horeb und beteten an das gegossene Bild
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
und verwandelten ihre Ehre in ein Gleichnis eines Ochsen, der Gras frißt.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Sie vergaßen Gottes, ihres Heilands, der so große Dinge in Ägypten getan hatte,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Wunder im Lande Hams und schreckliche Werke am Schilfmeer.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Und er sprach, er wolle sie vertilgen, wo nicht Mose, sein Auserwählter, in den Riß getreten wäre vor ihm, seinen Grimm abzuwenden, auf daß er sie nicht gar verderbte.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
und sie verachteten das liebe Land, sie glaubten seinem Wort nicht
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
und murrten in ihren Hütten; sie gehorchten der Stimme des HERRN nicht.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Und er hob auf seine Hand wider sie, daß er sie niederschlüge in der Wüste
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
und würfe ihren Samen unter die Heiden und zerstreute sie in die Länder.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Und sie hingen sich an den Baal-Peor und aßen von den Opfern der toten Götzen
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
und erzürnten ihn mit ihrem Tun; da brach auch die Plage unter sie.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Da trat Pinehas herzu und schlichtete die Sache; da ward der Plage gesteuert.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Das ward ihm gerechnet zur Gerechtigkeit für und für ewiglich.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Und sie erzürnten ihn am Haderwasser, und Mose ging es übel um ihretwillen.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Denn sie betrübten ihm sein Herz, daß ihm etliche Worte entfuhren.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Auch vertilgten sie die Völker nicht, wie sie doch der HERR geheißen hatte;
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
sondern sie mengten sich unter die Heiden und lernten derselben Werke
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
und dienten ihren Götzen; die wurden ihnen zum Fallstrick.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Und sie opferten ihre Söhne und ihre Töchter den Teufeln
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
und vergossen unschuldig Blut, das Blut ihrer Söhne und ihrer Töchter, die sie opferten den Götzen Kanaans, daß das Land mit Blutschulden befleckt ward;
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
und verunreinigten sich mit ihren Werken und wurden abgöttisch mit ihrem Tun.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Da ergrimmte der Zorn des HERRN über sein Volk, und er gewann einen Greuel an seinem Erbe
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
und gab sie in die Hände der Heiden, daß über sie herrschten, die ihnen gram waren.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Und ihre Feinde ängsteten sie; und sie wurden gedemütigt unter ihre Hände.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Er errettete sie oftmals; aber sie erzürnten ihn mit ihrem Vornehmen und wurden wenig um ihrer Missetat willen.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Und er sah ihre Not an, da er ihre Klage hörte,
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
und gedachte an seinen Bund, den er mit ihnen gemacht hatte; und es reute ihn nach seiner großen Güte,
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
und er ließ sie zur Barmherzigkeit kommen vor allen, die sie gefangen hatten.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Hilf uns, HERR, unser Gott, und bringe uns zusammen aus den Heiden, daß wir danken deinem heiligen Namen und rühmen dein Lob.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Gelobet sei der HERR, der Gott Israels, von Ewigkeit zu Ewigkeit, und alles Volk spreche: Amen, halleluja!

< Masalimo 106 >