< Masalimo 106 >
1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Alléluiah! Rendez grâces au Seigneur, parce qu'il est bon, parce que sa miséricorde est éternelle.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Qui dira la puissance du Seigneur, qui fera entendre toutes ses louanges?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Heureux ceux qui gardent ses jugements et qui font justice en tout temps!
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Souviens-toi de nous, Seigneur, avec ta bonté pour ton peuple; visite- nous avec ton salut;
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Afin que nous puissions avoir part aux biens de tes élus, nous réjouir de la joie de ton peuple, te glorifier avec ceux de ton héritage.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Nous avons péché avec nos pères, nous avons violé ta loi, nous avons commis l'iniquité.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Nos pères en Egypte ne comprirent point tes prodiges, et ils ne se souvinrent pas de l'abondance de ta miséricorde; et ils te provoquèrent, en arrivant à la mer Rouge.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Et il les sauva pour la gloire de son nom, et pour manifester sa puissance.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Et il menaça la mer Rouge, et elle fut desséchée; et il les ramena dans l'abîme, comme dans le désert.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Et il les sauva des mains de ceux qui les haïssaient, et il les racheta de la main de l'ennemi.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
L'eau couvrit ceux qui les opprimaient, et pas un d'eux n'échappa.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Et ils eurent foi en ses paroles, et ils chantèrent ses louanges.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Mais ils oublièrent bien vite ses œuvres; ils n'attendirent point son conseil.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Et ils furent pris de concupiscence dans la solitude, et ils tentèrent Dieu dans le désert sans eau.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Et il leur accorda ce qu'ils demandaient, et il envoya la satiété dans leur âme.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Et ils irritèrent Moïse dans le camp, et Aaron le saint du Seigneur.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
La terre s'ouvrit, et elle engloutit Dathan, et engouffra le rassemblement d'Abiron.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Et la flamme dévora leur synagogue, et le feu consuma les pécheurs.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Et ils se firent un veau en Choreb, et ils adorèrent une image sculptée.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Et ils échangèrent leur gloire contre la statue d'un veau qui se repaît de fourrage.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Ils oublièrent le Dieu qui les avait sauvés, qui avait fait de grandes choses en Egypte,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Des prodiges en la terre de Cham, et des actions terribles sur la mer Rouge.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Et il dit qu'il les exterminerait, si Moïse, son élu, ne s'était placé devant lui, et n'eût brisé l'idole, pour détourner sa fureur et l'empêcher de les détruire.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Et ils méprisèrent comme rien la terre désirable, et n'eurent point foi en la parole de Dieu.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Et ils murmurèrent sous leurs tentes, et n'écoutèrent point la voix du Seigneur!
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Et il leva la main sur eux pour les abattre dans le désert,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
Et pour rejeter leur race parmi les nations, et les disperser en diverses régions.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Et ils se prostituèrent à Belphégor, et ils mangèrent des victimes sacrifiées aux morts.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Et ils irritèrent Dieu par leurs désordres, et la ruine se multiplia chez eux.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Et Phinéès se leva, et il apaisa le Seigneur, et la plaie cessa.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Et cela lui fut imputé à justice, de génération en génération, dans tous les siècles.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Et ils irritèrent Dieu vers les eaux de contradiction, et Moïse eut à souffrir de leur part;
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Parce qu'ils avaient rempli son esprit d'une amertume qui s'échappa de ses lèvres.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Ils n'exterminèrent point les nations, comme le Seigneur le leur avait dit;
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Et ils se mêlèrent aux Gentils, et ils apprirent leurs œuvres,
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Et ils servirent leurs idoles, et ce fut pour eux un sujet de chute.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Et ils sacrifièrent aux démons leurs fils et leurs filles.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Et ils versèrent le sang innocent, le sang de leurs fils et de leurs filles, qu'ils immolèrent aux sculptures de Chanaan. Et la terre fut pleine de carnage et de sang.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Et elle fut souillée par leurs œuvres; et ils se prostituèrent en leurs passions.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Et le Seigneur s'enflamma de colère contre son peuple, et il eut en abomination son héritage.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Et il les livra aux mains de leurs ennemis, et ceux qui les haïssaient devinrent leurs maîtres.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Et leurs ennemis les opprimèrent, et ils furent humiliés sous leurs mains.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Souvent Dieu les sauva; mais ils l'irritèrent encore en leurs conseils, et ils furent humiliés dans leurs iniquités.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Et le Seigneur les vit en leurs tribulations, et il écouta leur prière.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Et il se souvint de son alliance, et il se repentit en la plénitude de sa miséricorde.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Et il leur accorda ses miséricordes, en face de ceux qui les retenaient captifs.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Sauve-nous, Seigneur notre Dieu, et rassemble-nous du milieu des Gentils, pour que nous proclamions ton saint nom et que nous mettions notre gloire à te louer.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Béni soit le Seigneur, Dieu d'Israël, dans tous les siècles des siècles, et tout le peuple dira: Ainsi soit-il! Ainsi soit-il!