< Masalimo 106 >
1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Alleluya. Kouleche ye to the Lord, for he is good; for his mercy is with outen ende.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Who schal speke the powers of the Lord; schal make knowun alle hise preisyngis?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Blessid ben thei that kepen dom; and doon riytfulnesse in al tyme.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Lord, haue thou mynde on vs in the good plesaunce of thi puple; visite thou vs in thin heelthe.
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
To se in the goodnesse of thi chosun men, to be glad in the gladnes of thi folk; that thou be heried with thin eritage.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
We han synned with oure fadris; we han do vniustli, we han do wickidnesse.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Oure fadris in Egipt vndirstoden not thi merueils; thei weren not myndeful of the multitude of thi merci. And thei stiynge in to the see, in to the reed see, terreden to wraththe;
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
and he sauede hem for his name, that `he schulde make knowun his power.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
And he departide the reed see, and it was dried; and he lede forth hem in the depthis of watris as in deseert.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
And he sauede hem fro the hond of hateris; and he ayen bouyte hem fro the hond of the enemye.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
And the watir hilide men troublynge hem; oon of hem abood not.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
And thei bileueden to hise wordis; and thei preisiden the heriynge of hym.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Thei hadden `soone do, thei foryaten hise werkis; and thei abididen not his councel.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
And thei coueitiden coueitise in deseert; and temptiden God in a place with out watir.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
And he yaf to hem the axyng of hem; and he sente fulnesse in to the soulis of hem.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
And thei wraththiden Moyses in the castels; Aaron, the hooli of the Lord.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
The erthe was opened, and swolewid Datan; and hilide on the congregacioun of Abiron.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
And fier brente an hiye in the synagoge of hem; flawme brente synneris.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
And thei maden a calf in Oreb; and worschipiden a yotun ymage.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
And thei chaungiden her glorie; in to the liknesse of a calf etynge hei.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Thei foryaten God, that sauede hem, that dide grete werkis in Egipt,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
merueils in the lond of Cham; feerdful thingis in the reed see.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
And God seide, that he wolde leese hem; if Moises, his chosun man, hadde not stonde in the brekyng of his siyt. That he schulde turne awei his ire; lest he loste hem.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
And thei hadden the desirable lond for nouyt, thei bileueden not to his word, and thei grutchiden in her tabernaclis;
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
thei herden not the vois of the Lord.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
And he reiside his hond on hem; to caste doun hem in desert.
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
And to caste awei her seed in naciouns; and to leese hem in cuntreis.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
And thei maden sacrifice to Belfagor; and thei eeten the sacrificis of deed beestis.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
And thei wraththiden God in her fyndyngis; and fallyng was multiplied in hem.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
And Fynees stood, and pleeside God; and the veniaunce ceesside.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
And it was arrettid to hym to riytfulnesse; in generacioun and in to generacioun, til in to with outen ende.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
And thei wraththiden God at the watris of ayenseiyng; and Moises was trauelid for hem, for thei maden bittere his spirit,
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
and he departide in his lippis.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Thei losten not hethen men; whiche the Lord seide to hem.
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
And thei weren meddlid among hethene men, and lerneden the werkis of hem,
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
and serueden the grauen ymagis of hem; and it was maad to hem in to sclaundre.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
And thei offriden her sones; and her douytris to feendis.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
And thei schedden out innocent blood, the blood of her sones and of her douytris; whiche thei sacrificiden to the grauun ymagis of Chanaan.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
And the erthe was slayn in bloodis, and was defoulid in the werkis of hem; and thei diden fornicacioun in her fyndyngis.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
And the Lord was wrooth bi strong veniaunce ayens his puple; and hadde abhominacioun of his eritage.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
And he bitook hem in to the hondis of hethene men; and thei that hatiden hem, weren lordis of hem.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
And her enemyes diden tribulacioun to hem, and thei weren mekid vndir the hondis of enemyes;
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
ofte he delyuerede hem. But thei wraththiden hym in her counsel; and thei weren maad low in her wickidnessis.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
And he siye, whanne thei weren set in tribulacioun; and he herde the preyer of hem.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
And he was myndeful of his testament; and it repentide hym bi the multitude of his merci.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
And he yaf hem in to mercies; in the siyt of alle men, that hadden take hem.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Oure Lord God, make thou vs saaf; and gadere togidere vs fro naciouns. That we knouleche to thin hooli name; and haue glorie in thi preisyng.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Blessid be the Lord God of Israel fro the world and til in to the world; and al the puple schal seye, Be it don, be it don.