< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Praise the LORD! Give thanks to the LORD, for he is good, for his loving kindness endures forever.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Who can utter the mighty acts of the LORD, or fully declare all his praise?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Blessed are those who keep justice. Blessed is one who does what is right at all times.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Remember me, LORD, with the favor that you show to your people. Visit me with your salvation,
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
that I may see the prosperity of your chosen, that I may rejoice in the gladness of your nation, that I may glory with your inheritance.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
We have sinned with our fathers. We have committed iniquity. We have done wickedly.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Our fathers didn’t understand your wonders in Egypt. They didn’t remember the multitude of your loving kindnesses, but were rebellious at the sea, even at the Sea of Suf.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Nevertheless he saved them for his name’s sake, that he might make his mighty power known.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
He rebuked the Sea of Suf also, and it was dried up; so he led them through the depths, as through a desert.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
He saved them from the hand of him who hated them, and redeemed them from the hand of the enemy.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
The waters covered their adversaries. There was not one of them left.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Then they believed his words. They sang his praise.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
They soon forgot his works. They didn’t wait for his counsel,
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
but gave in to craving in the desert, and tested God in the wasteland.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
He gave them their request, but sent leanness into their soul.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
They envied Moses also in the camp, and Aaron, the LORD’s holy one.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
The earth opened and swallowed up Dathan, and covered the company of Abiram.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
A fire was kindled in their company. The flame burned up the wicked.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
They made a calf in Horeb, and worshiped a molten image.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Thus they exchanged their glory for an image of a bull that eats grass.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
They forgot God, their Savior, who had done great things in Egypt,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
wondrous works in the land of Ham, and awesome things by the Sea of Suf.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Therefore he said that he would destroy them, had Moses, his chosen, not stood before him in the breach, to turn away his wrath, so that he wouldn’t destroy them.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Yes, they despised the pleasant land. They didn’t believe his word,
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
but murmured in their tents, and didn’t listen to the LORD’s voice.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Therefore he swore to them that he would overthrow them in the wilderness,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
that he would overthrow their offspring among the nations, and scatter them in the lands.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
They joined themselves also to Baal Peor, and ate the sacrifices of the dead.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Thus they provoked him to anger with their deeds. The plague broke in on them.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Then Phinehas stood up and executed judgment, so the plague was stopped.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
That was credited to him for righteousness, for all generations to come.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
They angered him also at the waters of Meribah, so that Moses was troubled for their sakes;
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
because they were rebellious against his spirit, he spoke rashly with his lips.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
They didn’t destroy the peoples, as the LORD commanded them,
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
but mixed themselves with the nations, and learned their works.
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
They served their idols, which became a snare to them.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Yes, they sacrificed their sons and their daughters to demons.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
They shed innocent blood, even the blood of their sons and of their daughters, whom they sacrificed to the idols of Canaan. The land was polluted with blood.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Thus they were defiled with their works, and prostituted themselves in their deeds.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Therefore the LORD burned with anger against his people. He abhorred his inheritance.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
He gave them into the hand of the nations. Those who hated them ruled over them.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Their enemies also oppressed them. They were brought into subjection under their hand.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
He rescued them many times, but they were rebellious in their counsel, and were brought low in their iniquity.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Nevertheless he regarded their distress, when he heard their cry.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
He remembered for them his covenant, and repented according to the multitude of his loving kindnesses.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
He made them also to be pitied by all those who carried them captive.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Save us, LORD, our God, gather us from among the nations, to give thanks to your holy name, to triumph in your praise!
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Blessed be the LORD, the God of Israel, from everlasting even to everlasting! Let all the people say, “Amen.” Praise the LORD!

< Masalimo 106 >