< Masalimo 106 >

1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Praise ye the LORD. O give thanks unto the LORD; for he is good: for his mercy [endureth] for ever.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Who can utter the mighty acts of the LORD, or shew forth all his praise?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Blessed are they that keep judgment, and he that doeth righteousness at all times.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Remember me, O LORD, with the favour that thou bearest unto thy people; O visit me with thy salvation:
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
That I may see the prosperity of thy chosen, that I may rejoice in the gladness of thy nation, that I may glory with thine inheritance.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
We have sinned with our fathers, we have committed iniquity, we have done wickedly.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Our fathers understood not thy wonders in Egypt; they remembered not the multitude of thy mercies; but were rebellious at the sea, even at the Red Sea.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Nevertheless he saved them for his name’s sake, that he might make his mighty power to be known.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
He rebuked the Red Sea also, and it was dried up: so he led them through the depths, as through a wilderness.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
And he saved them from the hand of him that hated them, and redeemed them from the hand of the enemy.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
And the waters covered their adversaries: there was not one of them left.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Then believed they his words; they sang his praise.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
They soon forgat his works; they waited not for his counsel:
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
But lusted exceedingly in the wilderness, and tempted God in the desert.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
And he gave them their request; but sent leanness into their soul.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
They envied Moses also in the camp, [and] Aaron the saint of the LORD.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
The earth opened and swallowed up Dathan, and covered the company of Abiram.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
And a fire was kindled in their company; the flame burned up the wicked.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
They made a calf in Horeb, and worshipped a molten image.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Thus they changed their glory for the likeness of an ox that eateth grass.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
They forgat God their saviour, which had done great things in Egypt;
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Wondrous works in the land of Ham, [and] terrible things by the Red Sea.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Therefore he said that he would destroy them, had not Moses his chosen stood before him in the breach, to turn away his wrath, lest he should destroy [them].
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Yea, they despised the pleasant land, they believed not his word;
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
But murmured in their tents, and hearkened not unto the voice of the LORD.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Therefore he lifted up his hand unto them, that he would overthrow them in the wilderness:
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
And that he would overthrow their seed among the nations, and scatter them in the lands.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
They joined themselves also unto Baal-peor, and ate the sacrifices of the dead.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Thus they provoked him to anger with their doings; and the plague brake in upon them.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Then stood up Phinehas, and executed judgment: and so the plague was stayed.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
And that was counted unto him for righteousness, unto all generations for evermore.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
They angered him also at the waters of Meribah, so that it went ill with Moses for their sakes:
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Because they were rebellious against his spirit, and he spake unadvisedly with his lips.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
They did not destroy the peoples, as the LORD commanded them;
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
But mingled themselves with the nations, and learned their works:
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
And they served their idols; which became a snare unto them:
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Yea, they sacrificed their sons and their daughters unto demons,
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
And shed innocent blood, even the blood of their sons and of their daughters, whom they sacrificed unto the idols of Canaan; and the land was polluted with blood.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Thus were they defiled with their works, and went a whoring in their doings.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Therefore was the wrath of the LORD kindled against his people, and he abhorred his inheritance.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
And he gave them into the hand of the nations; and they that hated them ruled over them.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Their enemies also oppressed them, and they were brought into subjection under their hand.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Many times did he deliver them; but they were rebellious in their counsel, and were brought low in their iniquity.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Nevertheless he regarded their distress, when he heard their cry:
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
And he remembered for them his covenant, and repented according to the multitude of his mercies.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
He made them also to be pitied of all those that carried them captives.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Save us, O LORD our God, and gather us from among the nations, to give thanks unto thy holy name, and to triumph in thy praise.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Blessed be the LORD, the God or Israel, from everlasting even to everlasting. And let all the people say, Amen. Praise ye the LORD.

< Masalimo 106 >