< Masalimo 106 >
1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Hallelujah! Give ye thanks unto Jehovah; for he is good; for his loving-kindness [endureth] for ever.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Who can utter the mighty acts of Jehovah? [who] can shew forth all his praise?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Blessed are they that keep justice, [and] he that doeth righteousness at all times.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Remember me, O Jehovah, with [thy] favour toward thy people; visit me with thy salvation:
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
That I may see the prosperity of thy chosen ones, that I may rejoice in the joy of thy nation, that I may glory with thine inheritance.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
We have sinned with our fathers, we have committed iniquity, we have done wickedly.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Our fathers in Egypt considered not thy wondrous works; they remembered not the multitude of thy loving-kindnesses; but they rebelled at the sea, at the Red Sea.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Yet he saved them for his name's sake, that he might make known his might.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
And he rebuked the Red Sea, and it dried up; and he led them through the deeps as through a wilderness.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
And he saved them from the hand of him that hated [them], and redeemed them from the hand of the enemy.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
And the waters covered their oppressors: there was not one of them left.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Then believed they his words; they sang his praise.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
They soon forgot his works; they waited not for his counsel:
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
And they lusted exceedingly in the wilderness, and tempted God in the desert.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Then he gave them their request, but sent leanness into their soul.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
And they envied Moses in the camp, [and] Aaron, the saint of Jehovah.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
The earth opened and swallowed up Dathan, and covered the company of Abiram;
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
And fire was kindled in their company; a flame burned up the wicked.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
They made a calf in Horeb, and did homage to a molten image;
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
And they changed their glory into the similitude of an ox that eateth grass.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
They forgot God their Saviour, who had done great things in Egypt,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Wondrous works in the land of Ham, terrible things by the Red Sea.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
And he said that he would destroy them, had not Moses, his chosen, stood before him in the breach, to turn away his fury, lest he should destroy [them].
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
And they despised the pleasant land; they believed not his word,
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
But murmured in their tents: they hearkened not unto the voice of Jehovah.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
And he lifted up his hand to them, that he would make them fall in the wilderness;
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
And that he would make their seed fall among the nations, and disperse them through the countries.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
And they joined themselves unto Baal-Peor, and ate the sacrifices of the dead;
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
And they provoked [him] to anger with their doings; and a plague broke out among them.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Then stood up Phinehas and executed judgment, and the plague was stayed;
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
And that was reckoned unto him for righteousness, from generation to generation, for evermore.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
And they moved him to wrath at the waters of Meribah, and it went ill with Moses on their account;
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
For they provoked his spirit, so that he spoke unadvisedly with his lips.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
They did not destroy the peoples, as Jehovah commanded them;
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
But they mingled with the nations, and learned their works;
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
And they served their idols; and they were a snare unto them:
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
And they sacrificed their sons and their daughters unto demons,
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
And shed innocent blood, the blood of their sons and of their daughters, whom they sacrificed unto the idols of Canaan; and the land was polluted with blood.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
And they were defiled with their works, and went a-whoring in their doings.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Then was the anger of Jehovah kindled against his people, and he abhorred his inheritance;
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
And he gave them into the hand of the nations; and they that hated them ruled over them:
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
And their enemies oppressed them, and they were brought into subjection under their hand.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Often did he deliver them; but as for them they provoked [him] by their counsel, and they were brought low by their iniquity.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
But he regarded their distress, when he heard their cry;
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
And he remembered for them his covenant, and repented according to the multitude of his loving-kindnesses;
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
And he caused them to find compassion of all those that had carried them captives.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Save us, Jehovah our God, and gather us from among the nations, to give thanks unto thy holy name, [and] to triumph in thy praise.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Blessed be Jehovah the God of Israel, from eternity and to eternity! And let all the people say, Amen! Hallelujah!