< Masalimo 106 >
1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
Priser Herren! thi han er god, thi hans Miskundhed varer evindelig.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
Hvo kan udsige Herrens vældige Gerninger, forkynde al hans Pris?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
Salige ere de, som holde over Ret, og den, som øver Retfærdighed alle Tider.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Herre! kom mig i Hu med din Kærlighed til dit Folk, besøg mig med din Frelse,
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
at jeg maa skue dine udvalgtes Lykke, glæde mig ved dit Folks Glæde, prise mig lykkelig i Samfund med din Arv.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
Vi have syndet med vore Fædre, vi have handlet ilde og gjort Ugudelighed.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
Vore Fædre i Ægypten vilde ikke forstaa dine underfulde Gerninger, de kom ikke din store Miskundhed i Hu, men vare genstridige ved Havet, ved det røde Hav.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Dog frelste han dem for sit Navns Skyld, for at kundgøre sin Magt.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Og han truede det røde Hav, og det blev tørt, og han lod dem gaa igennem Dybet som igennem Ørken.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Og han frelste dem af Avindsmandens Haand og genløste dem af Fjendens Haand.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
Og Vandene skjulte deres Modstandere, der blev ikke een tilovers af dem.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
Da troede de paa hans Ord, de sang hans Pris.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
Dog glemte de hans Gerninger snart, de biede ikke paa hans Raad.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Men de fik stor Begærlighed i Ørken og fristede Gud i det øde Land.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Da gav han dem det, de begærede, men lod deres Liv tæres hen.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Og de bare Avind imod Mose i Lejren, imod Aron, Herrens hellige.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Jorden oplod sig og opslugte Dathan, og den skjulte Abirams Hob.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
Og Ild flammede op iblandt deres Hob, en Lue fortærede de ugudelige.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
De dannede en Kalv ved Horeb og tilbade et støbt Billede.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Og de ombyttede deres Herlighed med Billedet af en Okse, som æder Urter.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
De glemte Gud, deres Frelser, som havde gjort store Ting i Ægypten,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
underfulde Gerninger i Kams Land, forfærdelige Ting ved det røde Hav.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Og han sagde, at han vilde ødelægge dem; dersom Mose, hans udvalgte, ikke havde stillet sig i Gabet for hans Ansigt, at afvende hans Vrede fra at ødelægge dem —!
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
De foragtede ogsaa det yndige Land, de troede ikke hans Ord.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Men de knurrede i deres Telte, de hørte ikke paa Herrens Røst.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Og han svor dem med oprakt Haand, at han vilde lade dem falde i Ørken,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
og at han vilde lade deres Afkom falde iblandt Hedningerne og bortstrø dem i Landene.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Og de bandt sig til Baal-Peor og aade af Ofrene til de døde Afguder.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
Og de opirrede ham med deres Idrætter, saa at en Plage brød løs paa dem,
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Da stod Pinehas frem og holdt Dom, og Plagen hørte op.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Og det blev regnet ham til Retfærdighed fra Slægt til Slægt evindelig.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
De fortørnede ham ogsaa ved Meribas Vand, og det gik Mose ilde for deres Skyld.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
Thi de vare genstridige imod hans Aand, og han talte ubetænksomt med sine Læber.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
De ødelagde ikke Folkene, om hvilke Herren havde sagt det til dem.
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Men de blandede sig med Hedningerne og lærte deres Gerninger.
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Og de tjente deres Afguder, og disse bleve dem til en Snare.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Og de ofrede deres Sønner og deres Døtre til Magterne.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Og de udøste uskyldigt Blod, deres Sønners og deres Døtres Blod, som de ofrede til Kanaans Afguder, og Landet vanhelligedes af Blodet.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
Og de besmittede sig ved deres Gerninger, og de bolede ved deres Idrætter.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Da optændtes Herrens Vrede imod hans Folk, og han fik en Vederstyggelighed til sin Arv.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Og han gav dem i Hedningernes Haand, og deres Avindsmænd herskede over dem.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
Og deres Fjender trængte dem, og de bleve ydmygede under deres Haand.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Han friede dem mange Gange; men de satte sig op imod ham i deres Raad, og de bleve nedtrykte for deres Misgerningers Skyld.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Dog saa han til dem, da de vare i Angest, idet han hørte deres Raab.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Og han kom sin Pagt i Hu, dem til Bedste, og det angrede ham efter hans store Miskundhed.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Og han lod dem finde Barmhjertighed hos alle dem, som havde bortført dem.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Frels os, Herre, vor Gud! og saml os fra Hedningerne, at vi kunne takke dit hellige Navn, rose os af din Pris!
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Lovet være Herren, Israels Gud, fra Evighed og indtil Evighed; og alt Folket siger: Amen. Halleluja!