< Masalimo 106 >
1 Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
BOEIPA te thangthen uh. Amah kah sitlohnah tah kumhal hil ham a then dongah BOEIPA te uem uh lah.
2 Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
BOEIPA kah thayung thamal te unim aka thui thai vetih amah koehnah te boeih aka yakming thai eh?
3 Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
A tuetang boeih dongah tiktamnah aka ngaithuen tih duengnah aka saii tah a yoethen pai saeh.
4 Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
Aw BOEIPA, na pilnam kah kolonah khuiah kai m'poek lamtah namah kah khangnah neh kai n'hip lah.
5 kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
Na coelh rhoek kah hnothen te hmuh sak ham, na namtu kah kohoenah dongah kohoe sak ham, na rho neh thangthen ham ni.
6 Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
A pa rhoek neh ka tholh uh dongah, paihaeh la ka boe uh.
7 Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
A pa rhoek loh Egypt ah nang kah khobaerhambae bangla cangbam uh pawt tih, na sitlohnah cungkuem te a poek uh pawt dongah, tuitunli kah carhaek li ah a koek uh.
8 Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
Tedae a ming neh a thayung thamal te ming sak hamla amih te a khang.
9 Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
Carhaek li te a ho tih a kak sak phoeiah tuidung longah khosoek bangla amih te a caeh puei.
10 Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
Te vaengah amih te a lunguet kut lamloh a khang tih thunkha kut lamkah a tlan.
11 Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
A rhal rhoek te tui loh a khuk uh tih pakhat kangna khaw sueng uh pawh.
12 Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
A olkhueh te a tangnah uh tih amah koehnah te a hlai uh.
13 Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
A bibi te koeloe a hnilh uh tih a oluen te rhing uh pawh.
14 Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
Te dongah khosoek ah hoehhamnah a pael uh tih khopong ah Pathen a noemcai uh.
15 Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
Amih kah huithuinah te a paek ngawn dae a hinglu dongah pimyet a tueih pah.
16 Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
Rhaehhmuen ah Moses taeng neh BOEIPA kah hlang cim Aron taengah thatlai uh.
17 Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
Diklai te ang tih Dathan te a dolh dongah Abiram hlangboel te khup a vuei.
18 Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
A hlangboel lakliah hmai loh rhong tih halang rhoek te hmaisai loh a hlawp.
19 Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
Horeb ah vaitoca mueihlawn a saii uh tih a bawk uh.
20 Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
Amih kah thangpomnah te rham aka ca vaitotal muei la a hoi uh.
21 Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
Egypt ah hno len a saii tih amih aka khang Pathen,
22 zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
Ham kho ah khobaerhambae aka saii, Carhaek li ah mueirhih aka saii te a hnilh uh.
23 Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
Amih te mitmoeng sak ham a ti vaengah a mikhmuh kah a puut ah a coelh Moses pai pawt koinih a kosi mael pawt vetih a phae pawn ni.
24 Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
Sahnaih khohmuen te a hnawt uh dongah a olkhueh te tangnah uh pawh.
25 Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
Amih kah dap khuiah cailak uh tih BOEIPA ol te hnatun uh pawh.
26 Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
Te dongah amih te khosoek ah cungku sak ham,
27 kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
Namtom taengah a tiingan cungku sak ham neh diklai ah thaekyak ham kut a thueng thil.
28 Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
Te dongah Baalpeor neh sun uh tih aka duek kah hmueih te a caak uh.
29 anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
A khoboe neh BOEIPA a veet uh dongah, amih taengah lucik a pung pah.
30 Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
Tedae Phinekha te thoo tih a thangthui daengah lucik khaw cing.
31 Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
Te vaengah anih te cadilcahma phoeikah cadilcahma ham kumhal hil duengnah la a nawt.
32 Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
Meribah tui taengah a thintoek uh bal tih amih kongah Moses te a talh.
33 pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
A mueihla te a koek uh dongah a ka nen khaw cal buengrhuet.
34 Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
Amih taengkah BOEIPA loh a uen bangla pilnam rhoek mitmoeng sak uh pawh.
35 Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
Tedae namtom rhoek neh pitpom uh hmaih tih amih kah bibi te a awt uh.
36 Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
Te dongah amamih ham hlaeh la aka poeh muei taengah tho a thueng uh.
37 Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
Te vaengah a ca huta khaw tongpa khaw rhaithae taengla a nawn uh.
38 Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
Kanaan muei taengah a nawn uh tih ommongsitoe thii, a ca tongpa neh a ca huta kah thii a long sak uh dongah thii loh diklai a poeih.
39 Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
A bibi neh a poeih uh tih a khoboe neh cukhalh uh.
40 Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
Te dongah a pilnam te BOEIPA kah thintoek loh sai coeng tih a rho te a tuei.
41 Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
Te vaengah amih te namtom kut ah a paek tih a lunguet loh amih te rhep a buem.
42 Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
A thunkha rhoek loh amih a nen uh tih a kut hmuiah a kunyun sakuh.
43 Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
Amih te koep koep puet a huul coeng dae amamih kah kopoek neh a koek uh dongah amamih kathaesainah neh tlumhmawn uh.
44 Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
Tedae amih kah a tamlung te a yaak vaengah amih kah rhal te a hmuh pah.
45 Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
Te vaengah a paipi te amih ham a poek pah tih a sitlohnah khuikah a sitlohnah cungkuem neh ko koep a hlawt.
46 Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
Te dongah amih aka sol rhoek boeih loh amih taengah haidamnah ham a paek.
47 Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
Kaimih kah Pathen BOEIPA kaimih he n'khang lamtah na ming cim uem ham neh nang koehnah dongah ka domyok ham khaw, namtom rhoek kut lamkah kaimih n'coi lah.
48 Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.
Israel Pathen, BOEIPA tah khosuen lamkah kumhal duela a yoethen pai tih pilnam boeih loh, “Amen, BOEIPA thangthen uh,” ti saeh.