< Masalimo 105 >

1 Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikirani pakati pa anthu a mitundu ina zimene Iye wachita.
Дякуйте Господу, кличте Ім'я́ Його́, серед наро́дів звіщайте про чи́ни Його!
2 Imbirani Iye, imbani matamando kwa Iyeyo; fotokozani za machitidwe ake onse odabwitsa.
Співайте Йому, грайте Йому, говоріть про всі чу́да Його́!
3 Munyadire dzina lake loyera; mitima ya iwo amene amafunafuna Yehova ikondwere.
Хваліться святим Його Йме́нням, хай ті́шиться серце шука́ючих Господа!
4 Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi yonse.
Пошу́куйте Господа й силу Його, лице Його за́вжди шукайте!
5 Kumbukirani zodabwitsa zimene Iye anazichita, zozizwitsa zake ndi maweruzo amene anapereka,
Пам'ятайте про чу́да Його, які Він учинив, про озна́ки Його та про при́суди уст Його,
6 inu zidzukulu za Abrahamu mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhika ake.
ви, насіння Авраама, раба Його, сини Яковові, вибра́нці Його́!
7 Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; maweruzo ake ali pa dziko lonse lapansi.
Він — Госпо́дь, Бог наш, по ці́лій землі Його при́суди!
8 Iyeyo amakumbukira pangano lake kwamuyaya, mawu amene analamula kwa mibado yonse,
Він пам'ятає наві́ки Свого заповіта, те слово, яке наказав був на тисячу родів,
9 pangano limene Iye anapanga ndi Abrahamu, lumbiro limene analumbira kwa Isake.
що склав Він його з Авраа́мом, і прися́гу Свою — для Ісака.
10 Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga zophunzitsa, kwa Israeli monga pangano lamuyaya:
Він поставив її за Зако́на для Якова, Ізраїлеві — заповітом навіки,
11 “Ndidzapereka kwa iwe dziko la Kanaani ngati gawo la cholowa chako.”
говорячи: „Я дам тобі Край ханаа́нський, частину спа́дщини для вас“!
12 Pamene iwo anali ngati anthu ochepa mʼchiwerengero, ochepa ndithu, ndiponso alendo mʼdzikolo,
Тоді їх було́ невелике число, нечисле́нні були та прихо́дьки на ній,
13 ankayendayenda kuchoka ku mtundu wina wa anthu ndi kupita ku mtundu wina, kuchoka mu ufumu wina kupita ku wina.
і ходили вони від наро́ду до наро́ду, від царства до іншого лю́ду.
14 Iye sanalole wina aliyense kuwapondereza; anadzudzula mafumu chifukwa cha iwo:
Не дозво́лив ніко́му Він кри́вдити їх, і за них Він царям докоря́в:
15 “Musakhudze odzozedwa anga; musachitire choyipa aneneri anga.”
„Не дото́ркуйтеся до Моїх помаза́нців, а пророкам Моїм не робі́те лихого!“
16 Iye anabweretsa njala pa dziko ndipo anawononga chakudya chonse;
І покликав Він голод на землю, всяке хлі́бне стебло́ полама́в.
17 Iyeyo anatumiza munthu patsogolo pawo, Yosefe anagulitsidwa ngati kapolo.
Перед їхнім обличчям Він мужа послав, — за раба Йо́сип про́даний був.
18 Iwo anavulaza mapazi ake ndi matangadza, khosi lake analiyika mʼzitsulo,
Кайда́нами му́чили но́ги його, залізо пройшло в його тіло,
19 mpaka zimene Iye ananeneratu zitakwaniritsidwa, mpaka mawu a Yehova ataonetsa kuti Iye ananena zoona.
аж до ча́су випо́внення сло́ва Його, — слово Господнє його було ви́явило.
20 Mfumu inatuma munthu kukamumasula, wolamulira wa mitundu ya anthu anamasula iyeyo.
Цар послав — і його розв'яза́в, воло́дар народів — і його був звільни́в.
21 Anamuyika kukhala wolamulira nyumba yake, wolamulira zonse zimene iye anali nazo,
Він настанови́в його паном над домом своїм, і воло́дарем над усім маєтком своїм,
22 kulangiza ana a mfumu monga ankafunira ndi kuphunzitsa nzeru akuluakulu.
щоб в'язни́в він його можновла́дців по волі своїй, а старших його умудря́в.
23 Tsono Israeli analowa mu Igupto; Yakobo anakhala monga mlendo mʼdziko la Hamu.
І Ізраїль прибув до Єги́пту, і Яків заме́шкав у Ха́мовім кра́ї.
24 Yehova anachulukitsa anthu ake; ndipo anachititsa kuti akhale ochuluka kwambiri kuposa adani awo;
А наро́д Свій Він сильно розмно́жив, і зробив був рясні́шим його від його ворогів.
25 amene mitima yawo anayitembenuza kuti idane ndi anthu ake, kukonzera chiwembu atumiki ake.
Він переміни́в їхнє серце, щоб народа Його ненави́діли, щоб брались на хи́трощі проти рабів Його.
26 Yehova anatuma Mose mtumiki wake, ndi Aaroni amene Iye anamusankha.
Він послав був Мойсея, Свого раба, Аарона, що вибрав його,
27 Iwo anachita zizindikiro zozizwitsa pakati pawo, zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.
— вони положили були серед них Його ре́чі знаме́нні, та чу́да у Ха́мовім кра́ї.
28 Yehova anatumiza mdima nasandutsa dziko kuti likhale la mdima. Koma anthuwo anakaniratu mawu a Yehova.
Він темно́ту наслав — і поте́мніло, і вони не проти́вились слову Його.
29 Yehova anasandutsa madzi awo kukhala magazi, kuchititsa kuti nsomba zawo zife.
Він перемінив їхню воду на кров, і вмори́в їхню рибу.
30 Dziko lawo linadzaza ndi achule amene analowa mʼzipinda zogona za olamulira awo.
Їхній край зарої́вся був жа́бами, навіть в поко́ях царів їхніх.
31 Iye anayankhula, ndipo kunabwera ntchentche zochuluka ndi nsabwe mʼdziko lawo lonse.
Він сказав — й прибули́ рої мух, воші в ці́лому о́бширі їхньому.
32 Iyeyo anatembenuza mvula yawo kukhala matalala, ndi zingʼaningʼani mʼdziko lawo lonse;
Він градом зробив їхній дощ, палю́чий огонь — на їхню землю.
33 Anagwetsa mitengo yawo ya mpesa ndi mitengo yawo ya mkuyu, nawononganso mitengo ina ya mʼdziko lawolo.
І Він повибивав виноград їхній та фіґове дерево їхнє, і дереви́ну на о́бширі їхньому повило́млював.
34 Iye anayankhula, ndipo dzombe linabwera, ziwala zosawerengeka;
Він сказав — і найшла сарана́ та гу́сінь без ліку, —
35 zinadya chilichonse chobiriwira cha mʼdziko lawo, zinadya zonse zotuluka mʼnthaka yawo.
усю ярину́ в їхнім кра́ї поже́рла, і плід землі їхньої з'їла.
36 Kenaka anakantha ana onse oyamba kubadwa a mʼdziko lawo, zipatso zoyamba za umunthu wawo wonse.
I Він повбивав усіх пе́рвістків в їхньому краї, поча́ток усякої їхньої сили.
37 Yehova anatulutsa Israeli, atatenga siliva ndi golide wambiri, ndipo pakati pa mafuko awo palibe mmodzi amene anafowoka.
І Він ви́провадив їх у срі́блі та в золоті, і серед їхніх племе́н не було́, хто б спіткну́вся.
38 Dziko la Igupto linakondwa pamene iwo anachoka, pakuti kuopsa kwa Israeli kunawagwera iwo.
Єгипет радів, коли вийшли вони, бо страх перед ними напа́в був на них.
39 Iye anatambasula mitambo ngati chofunda chawo, ndi moto owawunikira usiku.
Він хмару простяг на заслону, а огонь — на осві́тлення ночі.
40 Iwo anapempha, ndipo Iye anawabweretsera zinziri ndipo anawakhutitsa ndi chakudya chochokera kumwamba.
Зажадав був Ізраїль — і Він перепели́ці наслав, і хлібом небесним Він їх годува́в.
41 Iye anatsekula thanthwe, ndipo madzi anatuluka; ngati mtsinje anayenda mʼchipululu.
Відчинив був Він скелю — й лину́ла вода, потекли́ були ріки в пустинях,
42 Pakuti anakumbukira lonjezo lake loyera limene linaperekedwa kwa Abrahamu mtumiki wake.
бо Він пам'ятав за святе Своє слово, за Авраама, Свого раба.
43 Iye anatulutsa anthu ake akukondwera, osankhika ake akufuwula mwachimwemwe;
І Він з радістю вивів наро́д Свій, зо співом — вибра́нців Своїх,
44 Iye anawapatsa mayiko a anthu a mitundu ina ndipo anakhala olowamʼmalo a zimene ena anazivutikira,
І їм землю наро́дів роздав, і посі́ли вони працю лю́дів,
45 kuti iwo asunge malangizo ake ndi kutsatira malamulo ake. Tamandani Yehova.
щоб вико́нували Його за́повіді, та зако́ни Його берегли́! Алілу́я!

< Masalimo 105 >